Davide apempha Mulungu amthandize poyesedwa ndi zoipa
Salimo la Davide.
1 Yehova, ndaitana kwa Inu; ndifulumireni ine;
munditcherere khutu, pamene ndiitana kwa Inu.
2 Pemphero langa liikike ngati chofukiza pamaso panu;
kukweza manja anga kuikike ngati nsembe ya madzulo.
3 Muike mdindo pakamwa panga, Yehova;
sungani pakhomo pa milomo yanga.
4 Mtima wanga usalinge kuchinthu choipa,
kuchita ntchito zoipa
ndi anthu akuchita zopanda pake;
ndipo ndisadye zankhuli zao.
5 Akandipanda munthu wolungama ndidzati nchifundo:
akandidzudzula, ndidzakuyesa mafuta a pamutu;
mutu wanga usakane:
Pakuti pangakhale posautsidwa iwo ndidzawapempherera.
6 Oweruza ao anagwetseka pambali pa thanthwe;
nadzamva mau anga kuti ndiwo okondweretsa.
7 Mafupa athu amwazika pakamwa pa manda,
monga ngati akumba nanyimphula nthaka yapansi.
8 Pakuti maso anga apenya kwanu, Yehova Ambuye;
ndithawira kwa Inu; musataye moyo wanga.
9 Mundisunge ndisagwe mumsampha ananditcherawo,
ndisakodwe m’makwekwe a iwo ochita zopanda pake.
10 Oipa agwe pamodzi m’maukonde ao,
kufikira nditapitirira ine.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/141-36576f5f05d631c1d64279db9e575199.mp3?version_id=1068—