Categories
MASALIMO

MASALIMO 141

Davide apempha Mulungu amthandize poyesedwa ndi zoipa

Salimo la Davide.

1 Yehova, ndaitana kwa Inu; ndifulumireni ine;

munditcherere khutu, pamene ndiitana kwa Inu.

2 Pemphero langa liikike ngati chofukiza pamaso panu;

kukweza manja anga kuikike ngati nsembe ya madzulo.

3 Muike mdindo pakamwa panga, Yehova;

sungani pakhomo pa milomo yanga.

4 Mtima wanga usalinge kuchinthu choipa,

kuchita ntchito zoipa

ndi anthu akuchita zopanda pake;

ndipo ndisadye zankhuli zao.

5 Akandipanda munthu wolungama ndidzati nchifundo:

akandidzudzula, ndidzakuyesa mafuta a pamutu;

mutu wanga usakane:

Pakuti pangakhale posautsidwa iwo ndidzawapempherera.

6 Oweruza ao anagwetseka pambali pa thanthwe;

nadzamva mau anga kuti ndiwo okondweretsa.

7 Mafupa athu amwazika pakamwa pa manda,

monga ngati akumba nanyimphula nthaka yapansi.

8 Pakuti maso anga apenya kwanu, Yehova Ambuye;

ndithawira kwa Inu; musataye moyo wanga.

9 Mundisunge ndisagwe mumsampha ananditcherawo,

ndisakodwe m’makwekwe a iwo ochita zopanda pake.

10 Oipa agwe pamodzi m’maukonde ao,

kufikira nditapitirira ine.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/141-36576f5f05d631c1d64279db9e575199.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *