Davide apempha Mulungu amlanditse kwa mdani woipa wamphamvu
Kwa Mkulu wa Nyimbo: Salimo la Davide.
1 Ndilanditseni, Yehova, kwa munthu woipa;
ndisungeni kwa munthu wachiwawa;
2 amene adzipanga zoipa mumtima mwao;
masiku onse amemeza nkhondo.
3 Anola lilime lao ngati njoka;
pansi pa milomo yao pali ululu wa mphiri.
4 Ndilindireni Yehova, ndisalowe m’manja mwa woipa;
ndisungeni kwa munthu wachiwawa;
kwa iwo akuti akankhe mapazi anga.
5 Odzikuza ananditchera msampha, nandibisira zingwe;
anatcha ukonde m’mphepete mwa njira;
ananditchera makwekwe.
6 Ndinati kwa Yehova, Inu ndinu Mulungu wanga;
munditcherere khutu mau a kupemba kwanga, Yehova.
7 Yehova Ambuye, ndinu mphamvu ya chipulumutso changa,
munandiphimba mutu wanga tsiku lakulimbana nkhondo.
8 Yehova, musampatse woipa zokhumba iye;
musamthandize zodzipanga zake; angadzikuze.
9 Kunena za mutu wao wa iwo akundizinga,
choipa cha milomo yao chiwaphimbe.
10 Makala amoto awagwere;
aponyedwe kumoto;
m’maenje ozama, kuti asaukenso.
11 Munthu wamlomo sadzakhazikika padziko lapansi;
choipa chidzamsaka munthu wachiwawa kuti chimgwetse.
12 Ndidziwa kuti Yehova adzanenera wozunzika mlandu,
ndi kuweruzira aumphawi.
13 Indedi, olungama adzayamika dzina lanu;
oongoka mtima adzakhala pamaso panu.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/140-f00ee044309bcb1491e964d9efe48d2e.mp3?version_id=1068—