Anthu oipadi
Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide.
1 Wauchitsiru amati mumtima mwake, Kulibe Mulungu.
Achita zovunda, achita ntchito zonyansa;
kulibe wakuchita bwino.
2 Yehova mu Mwamba anaweramira pa ana a anthu,
kuti aone ngati aliko wanzeru,
wakufuna Mulungu.
3 Anapatuka onse; pamodzi anavunda mtima;
palibe wakuchita bwino ndi mmodzi yense.
4 Kodi onse ochita zopanda pake sadziwa kanthu?
Pakudya anthu anga monga akudya mkate,
ndipo saitana pa Yehova.
5 Pamenepa anaopaopatu,
pakuti Mulungu ali mu mbadwo wa wolungama.
6 Munyazitsa uphungu wa wozunzika,
koma Yehova ndiye pothawira pake.
7 Mwenzi chipulumutso cha Israele chitachokera kuZiyoni!
Pakubweretsa Yehova anthu ake a m’nsinga,
pamenepo adzakondwera Yakobo, nadzasekera Israele.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/14-077b876ad14e0f22bfb7d2de2c9b5075.mp3?version_id=1068—