Categories
MASALIMO

MASALIMO 14

Anthu oipadi

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide.

1 Wauchitsiru amati mumtima mwake, Kulibe Mulungu.

Achita zovunda, achita ntchito zonyansa;

kulibe wakuchita bwino.

2 Yehova mu Mwamba anaweramira pa ana a anthu,

kuti aone ngati aliko wanzeru,

wakufuna Mulungu.

3 Anapatuka onse; pamodzi anavunda mtima;

palibe wakuchita bwino ndi mmodzi yense.

4 Kodi onse ochita zopanda pake sadziwa kanthu?

Pakudya anthu anga monga akudya mkate,

ndipo saitana pa Yehova.

5 Pamenepa anaopaopatu,

pakuti Mulungu ali mu mbadwo wa wolungama.

6 Munyazitsa uphungu wa wozunzika,

koma Yehova ndiye pothawira pake.

7 Mwenzi chipulumutso cha Israele chitachokera kuZiyoni!

Pakubweretsa Yehova anthu ake a m’nsinga,

pamenepo adzakondwera Yakobo, nadzasekera Israele.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/14-077b876ad14e0f22bfb7d2de2c9b5075.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *