Categories
MASALIMO

MASALIMO 138

Davide ayamika Mulungu pa kukhulupirika kwake, naneneratu kuti mafumu onse adzatero

Salimo la Davide.

1 Ndidzakuyamikani ndi mtima wanga wonse;

ndidzaimba zakukulemekezani patsogolo pa milungu.

2 Ndidzagwadira kuloza ku Kachisi wanu woyera,

ndi kuyamika dzina lanu,

chifukwa cha chifundo chanu ndi choonadi chanu;

popeza munakuzitsa mau anu koposa dzina lanu lonse.

3 Tsiku loitana ine, munandiyankha,

munandilimbitsa ndi mphamvu m’moyo mwanga.

4 Mafumu onse a padziko lapansi adzakuyamikani,

Yehova, popeza adamva mau a pakamwa panu.

5 Ndipo adzaimbira njira za Yehova;

pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.

6 Angakhale Yehova ngwokwezeka, apenyanso wopepukayo;

koma wodzikuza amdziwira kutali.

7 Ndingakhale ndiyenda pakati pa nsautso, mudzandipatsa moyo;

mudzatambasula dzanja lanu pa mkwiyo wa adani anu,

ndipo dzanja lanu lamanja lidzandipulumutsa.

8 Yehova adzanditsirizira za kwa ine:

Chifundo chanu, Yehova, chifikira kunthawi zonse:

Musasiye ntchito za manja anu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/138-baf99d1c1610bf2b5dde57b52d513be1.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *