Categories
MASALIMO

MASALIMO 136

Mulungu alemekezedwe pa chifundo chake

1 Yamikani Yehova pakuti ndiye wabwino;

pakuti chifundo chake nchosatha.

2 Yamikani Mulungu wa milungu;

pakuti chifundo chake nchosatha.

3 Yamikani Mbuye wa ambuye;

pakuti chifundo chake nchosatha.

4 Amene yekha achita zodabwitsa zazikulu;

pakuti chifundo chake nchosatha.

5 Amene analenga zakumwamba mwanzeru;

pakuti chifundo chake nchosatha.

6 Amene anayala dziko lapansi pamwamba pamadzi;

pakuti chifundo chake nchosatha.

7 Amene analenga miuni yaikulu;

pakuti chifundo chake nchosatha.

8 Dzuwa liweruze usana;

pakuti chifundo chake nchosatha.

9 Mwezi ndi nyenyezi ziweruze usiku;

pakuti chifundo chake nchosatha.

10 Iye amene anapandira Aejipito ana ao oyamba;

pakuti chifundo chake nchosatha.

11 Natulutsa Israele pakati pao;

pakuti chifundo chake nchosatha.

12 Ndi dzanja lamphamvu, ndi mkono wotambasuka;

pakuti chifundo chake nchosatha.

13 Amene anagawa magawo Nyanja Yofiira;

pakuti chifundo chake nchosatha.

14 Napititsa Israele pakati pake;

pakuti chifundo chake nchosatha.

15 NakhuthulaFaraondi khamu lake mu Nyanja Yofiira:

pakuti chifundo chake nchosatha.

16 Amene anatsogolera anthu ake m’chipululu;

pakuti chifundo chake nchosatha.

17 Amene anapanda mafumu aakulu;

pakuti chifundo chake nchosatha.

18 Ndipo anawapha mafumu omveka;

pakuti chifundo chake nchosatha.

19 Sihoni mfumu ya Aamori;

pakuti chifundo chake nchosatha.

20 Ndi Ogi mfumu ya Basani;

pakuti chifundo chake nchosatha.

21 Ndipo anapereka dziko lao likhale cholowa;

pakuti chifundo chake nchosatha.

22 Cholowa cha kwa Israele mtumiki wake;

pakuti chifundo chake nchosatha.

23 Amene anatikumbukira popepuka ife;

pakuti chifundo chake nchosatha.

24 Natikwatula kwa otisautsa;

pakuti chifundo chake nchosatha.

25 Ndiye wakupatsa nyama zonse chakudya;

pakuti chifundo chake nchosatha.

26 Yamikani Mulungu wa Kumwamba,

pakuti chifundo chake nchosatha.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/136-3ce0d50841b7431da42362b695c5d946.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *