Categories
MASALIMO

MASALIMO 133

Chikondano cha abale ndi chokoma

Nyimbo yokwerera; ya Davide.

1 Onani, nkokoma ndi kokondweretsa ndithu

kuti abale akhale pamodzi!

2 Ndiko ngati mafuta a mtengo wake pamutu,

akutsikira kundevu,

inde kundevu za Aroni;

akutsikira kumkawo wa zovala zake.

3 Ngati mame a ku Heremoni,

akutsikira pa mapiri aZiyoni.

Pakuti pamenepo Yehova analamulira dalitsolo,

ndilo moyo womka muyaya.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/133-de1654ae8ff13fcab0f2dd7436667ef5.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *