Categories
MASALIMO

MASALIMO 132

Davide asamalira Kachisi ndi likasa. Lonjezano la Mulungu

Nyimbo yokwerera.

1 Yehova, kumbukirani Davide

kuzunzika kwake konse.

2 Kuti analumbira Yehova,

nawindira Wamphamvuyo wa Yakobo, ndi kuti,

3 Ngati ndidzalowa pakhomo pa nyumba yanga,

ngati ndidzakwera pa kama logonapo;

4 ngati ndidzalola maso anga agone,

kapena zikope zanga ziodzere;

5 kufikira nditapezera Yehova malo,

chokhalamo Wamphamvuyo wa Yakobo?

6 Taonani, tinachimva mu Efurata;

tinachipeza kuchidikha cha kunkhalango.

7 Tidzalowa mokhalamo Iye;

tidzagwadira kumpando wa mapazi ake.

8 Ukani, Yehova, lowani ku mpumulo wanu;

Inu ndi hema wa mphamvu yanu.

9 Ansembe anu avale chilungamo;

ndi okondedwa anu afuule mokondwera.

10 Chifukwa cha Davide mtumiki wanu

musabweze nkhope ya wodzozedwa wanu.

11 Yehova analumbira Davide zoona;

sadzalibweza; ndi kuti,

Wa iwo okhala zipatso za thupi lako

ndidzaika pa mpando wachifumu wako.

12 Ana ako akasungachipanganochanga

ndi mboni yanga imene ndidzawaphunzitsa,

ana aonso adzakhala pa mpando wanu kunthawi zonse,

13 pakuti Yehova anasankhaZiyoni;

analikhumba likhale pokhala pake; ndi kuti,

14 Pampumulo panga mpano posatha,

Pano ndidzakhala; pakuti ndakhumbapo.

15 Ndidzadalitsatu chakudya chake;

aumphawi ake ndidzawakhutitsa ndi mkate.

16 Ndipo ansembe ake ndidzawaveka ndi chipulumutso:

Ndi okondedwa ake adzafuulitsa mokondwera.

17 Apo ndidzaphukitsira Davide nyanga;

ndakonzeratu wodzozedwa wanga nyali.

18 Ndidzawaveka adani ake ndi manyazi;

koma pa iyeyu korona wake adzamveka.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/132-1a766d8dc23c1a98cb39b86003c887b4.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *