Categories
MASALIMO

MASALIMO 130

Pemphero lakuti akhululukidwe

Nyimbo yokwerera.

1 M’mozamamo ndinakufuulirani, Yehova.

2 Ambuye, imvani liu langa;

makutu anu akhale chimverere

mau a kupemba kwanga.

3 Mukasunga mphulupulu, Yehova,

adzakhala chilili ndani, Ambuye?

4 Koma kwa Inu kuli chikhululukiro,

kuti akuopeni.

5 Ndilindira Yehova, moyo wanga ulindira,

ndiyembekeza mau ake.

6 Moyo wanga uyang’anira Ambuye,

koposa alonda matanda kucha;

inde koposa alonda matanda kucha.

7 Israele, uyembekezere Yehova;

chifukwa kwa Yehova kuli chifundo,

kwaonso kuchulukira chiombolo.

8 Ndipo adzaombola Israele

ku mphulupulu zake zonse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/130-08ede17c17095cb89fbacd5a4d727f95.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *