Categories
MASALIMO

MASALIMO 13

Munkhawa athawira Mulungu namkhulupirira

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide.

1 Mudzandiiwala chiiwalire, Yehova, kufikira liti?

Mudzandibisira ine nkhope yanu kufikira liti?

2 Ndidzachita uphungu m’moyo mwanga kufikira liti,

pokhala ndi chisoni m’mtima mwanga tsiku lonse?

Adzandiukira ine mdani wanga kufikira liti?

3 Penyani, ndiyankheni, Yehova Mulungu wanga.

Penyetsani maso anga, kuti ndingagone tulo ta imfa;

4 kuti anganene mdani wanga, Ndamgonjetsa;

ndipo angakondwere otsutsana nane posunthika ine.

5 Koma ine ndakhulupirira pa chifundo chanu;

mtima wanga udzakondwera nacho chipulumutso chanu.

6 Ndidzaimbira Yehova,

pakuti anandichitira zokoma.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/13-9cde76954810ab1f67a49fbbdcdf3261.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *