Munkhawa athawira Mulungu namkhulupirira
Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide.
1 Mudzandiiwala chiiwalire, Yehova, kufikira liti?
Mudzandibisira ine nkhope yanu kufikira liti?
2 Ndidzachita uphungu m’moyo mwanga kufikira liti,
pokhala ndi chisoni m’mtima mwanga tsiku lonse?
Adzandiukira ine mdani wanga kufikira liti?
3 Penyani, ndiyankheni, Yehova Mulungu wanga.
Penyetsani maso anga, kuti ndingagone tulo ta imfa;
4 kuti anganene mdani wanga, Ndamgonjetsa;
ndipo angakondwere otsutsana nane posunthika ine.
5 Koma ine ndakhulupirira pa chifundo chanu;
mtima wanga udzakondwera nacho chipulumutso chanu.
6 Ndidzaimbira Yehova,
pakuti anandichitira zokoma.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/13-9cde76954810ab1f67a49fbbdcdf3261.mp3?version_id=1068—