Israele asautsidwa koma osafafanizidwa
Nyimbo yokwerera.
1 Anandisautsa kawirikawiri kuyambira ubwana wanga,
anene tsono Israele;
2 Anandisautsa kawirikawiri kuyambira ubwana wanga;
koma sanandilake.
3 Olima analima pamsana panga;
anatalikitsa mipere yao.
4 Yehova ndiye wolungama;
anadulatu zingwe za oipa.
5 Achite manyazi nabwerere m’mbuyo.
Onse akudana nayeZiyoni.
6 Akhale ngati udzu womera patsindwi,
wakufota asanauzule;
7 umene womweta sadzaza nao dzanja lake,
kapena womanga mitolo sakupatira manja.
8 Angakhale opitirirapo sanena,
Dalitso la Mulungu likhale pa inu;
tikudalitsani m’dzina la Yehova.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/129-93250a4a1c17089c758d1fec58b2d20a.mp3?version_id=1068—