Categories
MASALIMO

MASALIMO 127

Madalitso onse, a m’banja omwe, achokera kwa Mulungu

Nyimbo yokwerera; ya Solomoni.

1 Akapanda kumanga nyumba Yehova,

akuimanga agwiritsa ntchito chabe;

akapanda kusunga mzinda Yehova,

mlonda adikira chabe.

2 Kuli chabe kwa inu kulawirira mamawa ndi kusagonerapo madzulo,

kudya mkate wosautsa kuupeza;

kuli tero kuti izi apatsa okondedwa ake ngati m’tulo.

3 Taonani, ana ndiwo cholowa cha kwa Yehova;

chipatso cha m’mimba ndicho mphotho yake.

4 Ana a ubwana wake wa munthu

akunga mivi m’dzanja lake la chiphona.

5 Wodala munthu amene anadzaza nayo phodo lake:

sadzachita manyazi iwo,

pakulankhula nao adani kuchipata.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/127-eeeab4dcd9f3f75aeebe2f4be6f88302.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *