Ayamikira mokondwerera kuti Mulungu anabweza ukapolo wao
Nyimbo yokwerera.
1 Pobweza Yehova ukapolo waZiyoni,
tinakhala ngati anthu akulota.
2 Pamenepo pakamwa pathu panadzala ndi kuseka,
ndi lilime lathu linafuula mokondwera;
pamenepo anati kwaamitundu,
Yehova anawachitira iwo zazikulu.
3 Yehova anatichitira ife zazikulu;
potero tikhala okondwera.
4 Bwezani ukapolo wathu, Yehova,
ngati mitsinje ya kumwera.
5 Akubzala ndi misozi adzatuta ndi kufuula mokondwera.
6 Iye amene ayendayenda nalira, ponyamula mbeu yakufesa;
adzabweranso ndithu ndi kufuula mokondwera,
alikunyamula mitolo yake.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/126-3263cbbe85cce41a2b4edb42773efe99.mp3?version_id=1068—