Categories
MASALIMO

MASALIMO 126

Ayamikira mokondwerera kuti Mulungu anabweza ukapolo wao

Nyimbo yokwerera.

1 Pobweza Yehova ukapolo waZiyoni,

tinakhala ngati anthu akulota.

2 Pamenepo pakamwa pathu panadzala ndi kuseka,

ndi lilime lathu linafuula mokondwera;

pamenepo anati kwaamitundu,

Yehova anawachitira iwo zazikulu.

3 Yehova anatichitira ife zazikulu;

potero tikhala okondwera.

4 Bwezani ukapolo wathu, Yehova,

ngati mitsinje ya kumwera.

5 Akubzala ndi misozi adzatuta ndi kufuula mokondwera.

6 Iye amene ayendayenda nalira, ponyamula mbeu yakufesa;

adzabweranso ndithu ndi kufuula mokondwera,

alikunyamula mitolo yake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/126-3263cbbe85cce41a2b4edb42773efe99.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *