Mulungu yekha walanditsa anthu ake
Nyimbo yokwerera; ya Davide.
1 Akadapanda kukhala nafe Yehova,
anene tsono Israele;
2 Akadapanda kukhala nafe Yehova,
pakutiukira anthu:
3 Akadatimeza amoyo,
potipsera mtima wao.
4 Akadatimiza madziwo,
mtsinje ukadapita pa moyo wathu;
5 madzi odzikuza akadapita pa moyo wathu.
6 Alemekezedwe Yehova,
amene sanatipereke kumano kwao tikhale chakudya chao.
7 Moyo wathu unaonjoka ngati mbalame mu msampha wa msodzi;
msampha unathyoka ndi ife tinaonjoka.
8 Thandizo lathu lili m’dzina la Yehova,
wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/124-2ff8b83e597e46994d314767b3d637d9.mp3?version_id=1068—