Categories
MASALIMO

MASALIMO 124

Mulungu yekha walanditsa anthu ake

Nyimbo yokwerera; ya Davide.

1 Akadapanda kukhala nafe Yehova,

anene tsono Israele;

2 Akadapanda kukhala nafe Yehova,

pakutiukira anthu:

3 Akadatimeza amoyo,

potipsera mtima wao.

4 Akadatimiza madziwo,

mtsinje ukadapita pa moyo wathu;

5 madzi odzikuza akadapita pa moyo wathu.

6 Alemekezedwe Yehova,

amene sanatipereke kumano kwao tikhale chakudya chao.

7 Moyo wathu unaonjoka ngati mbalame mu msampha wa msodzi;

msampha unathyoka ndi ife tinaonjoka.

8 Thandizo lathu lili m’dzina la Yehova,

wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/124-2ff8b83e597e46994d314767b3d637d9.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *