Categories
MASALIMO

MASALIMO 123

Pemphero la wonyozedwa

Nyimbo yokwerera.

1 Ndikweza maso anga kwa Inu,

kwa Inu wakukhala kumwamba.

2 Taonani, monga maso a anyamata

ayang’anira dzanja la ambuye wao,

monga maso a adzakazi

ayang’anira dzanja la mbuye wao wamkazi:

Momwemo maso athu ayang’anira Yehova Mulungu wathu,

kufikira atichitira chifundo.

3 Mutichitire chifundo, Yehova, mutichitire chifundo;

pakuti takhuta kwambiri ndi mnyozo.

4 Moyo wathu wakhuta ndithu

ndi kuseka kwa iwo osasowa kanthu,

ndi mnyozo wa odzikuza.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/123-3cf70daca6d6cb1ca6b207ff6ebd2c65.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *