Apempherera mtendere wa Yerusalemu
Nyimbo yokwerera; ya Davide.
1 Ndinakondwera m’mene ananena nane,
Tiyeni kunyumba ya Yehova.
2 Mapazi athu alinkuima
m’zipata zanu,Yerusalemu
3 Yerusalemu anamangidwa
ngati mzinda woundana bwino:
4 Kumene akwerako mafuko, ndiwo mafuko a Yehova;
akhale mboni ya kwa Israele, Ayamike dzina la Yehova.
5 Pakuti pamenepo anaika mipando ya chiweruzo,
mipando ya nyumba ya Davide.
6 Mupempherere mtendere wa Yerusalemu;
akukonda inu adzaona phindu.
7 M’linga mwako mukhale mtendere,
m’nyumba za mafumu mukhale phindu.
8 Chifukwa cha abale anga ndi mabwenzi anga,
ndidzanena tsopano, Mukhale mtendere mwa inu.
9 Chifukwa cha nyumba ya Yehova Mulungu wathu
ndidzakufunira zokoma.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/122-04dd1aec5107e11f98773d32fe0bf372.mp3?version_id=1068—