Categories
MASALIMO

MASALIMO 122

Apempherera mtendere wa Yerusalemu

Nyimbo yokwerera; ya Davide.

1 Ndinakondwera m’mene ananena nane,

Tiyeni kunyumba ya Yehova.

2 Mapazi athu alinkuima

m’zipata zanu,Yerusalemu

3 Yerusalemu anamangidwa

ngati mzinda woundana bwino:

4 Kumene akwerako mafuko, ndiwo mafuko a Yehova;

akhale mboni ya kwa Israele, Ayamike dzina la Yehova.

5 Pakuti pamenepo anaika mipando ya chiweruzo,

mipando ya nyumba ya Davide.

6 Mupempherere mtendere wa Yerusalemu;

akukonda inu adzaona phindu.

7 M’linga mwako mukhale mtendere,

m’nyumba za mafumu mukhale phindu.

8 Chifukwa cha abale anga ndi mabwenzi anga,

ndidzanena tsopano, Mukhale mtendere mwa inu.

9 Chifukwa cha nyumba ya Yehova Mulungu wathu

ndidzakufunira zokoma.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/122-04dd1aec5107e11f98773d32fe0bf372.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *