Categories
MASALIMO

MASALIMO 120

Apempha Mulungu amlanditse pa omnamiza

Nyimbo yokwerera.

1 Ndinafuulira kwa Yehova mu msauko wanga,

ndipo anandivomereza.

2 Yehova, landitsani moyo wanga kumilomo ya mabodza,

ndi kulilime lonyenga.

3 Adzakuninkhanji, adzakuonjezeranji,

lilime lonyenga iwe?

4 Mivi yakuthwa ya chiphona,

ndi makala tsanya.

5 Tsoka ine, kuti ndili mlendo mu Meseki,

kuti ndigonera m’mahema a Kedara!

6 Moyo wanga unakhalitsa nthawi

pamodzi ndi iye wakudana nao mtendere.

7 Ine ndikuti, Mtendere;

koma polankhula ine, iwowa akuti, Nkhondo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/120-9446c9b8452065a4e6d585a5fdd35301.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *