Categories
MASALIMO

MASALIMO 12

Anthu ndi amabodza, Mulungu ndiye woona

Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Seminiti. Salimo la Davide.

1 Pulumutsani, Yehova; pakuti wofatsa wasowa;

pakuti okhulupirika achepa mwa ana a anthu.

2 Amanena za bodza munthu yense ndi mnansi wake,

amanena ndi mlomo wothyasika, ndi mitima iwiri.

3 Yehova adzadula milomo yonse yothyasika,

lilime lakudzitamandira;

4 amene amati, Ndi lilime lathu tidzaposa;

milomo yathu nja ife eni; mbuye wa pa ife ndani?

5 Chifukwa cha kupasuka kwa ozunzika,

chifukwa cha kuusa moyo kwa aumphawi,

ndiuka tsopano, ati Yehova;

ndidzamlonga mosungika muja alakalakamo.

6 Mau a Yehova ndi mau oona;

ngatisilivawoyenga m’ng’anjo yadothi,

yoiyeretsa kasanu ndi kawiri.

7 Mudzawasunga, Yehova,

mudzawatchinjirizira mbadwo uno kunthawi zonse.

8 Oipa amayenda mozungulirazungulira,

potamanda iwo chonyansa mwa ana a anthu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/12-7c5bb2f4a31918aa5895fc65a425fe52.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *