Anthu ndi amabodza, Mulungu ndiye woona
Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Seminiti. Salimo la Davide.
1 Pulumutsani, Yehova; pakuti wofatsa wasowa;
pakuti okhulupirika achepa mwa ana a anthu.
2 Amanena za bodza munthu yense ndi mnansi wake,
amanena ndi mlomo wothyasika, ndi mitima iwiri.
3 Yehova adzadula milomo yonse yothyasika,
lilime lakudzitamandira;
4 amene amati, Ndi lilime lathu tidzaposa;
milomo yathu nja ife eni; mbuye wa pa ife ndani?
5 Chifukwa cha kupasuka kwa ozunzika,
chifukwa cha kuusa moyo kwa aumphawi,
ndiuka tsopano, ati Yehova;
ndidzamlonga mosungika muja alakalakamo.
6 Mau a Yehova ndi mau oona;
ngatisilivawoyenga m’ng’anjo yadothi,
yoiyeretsa kasanu ndi kawiri.
7 Mudzawasunga, Yehova,
mudzawatchinjirizira mbadwo uno kunthawi zonse.
8 Oipa amayenda mozungulirazungulira,
potamanda iwo chonyansa mwa ana a anthu.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/12-7c5bb2f4a31918aa5895fc65a425fe52.mp3?version_id=1068—