Wa Salimo alemekeza Mulungu womlanditsa m’manja mwa adani
1 Yamikani Yehova; pakuti Iye ndiye wabwino;
pakuti chifundo chake nchosatha.
2 Anene tsono Israele,
kuti chifundo chake nchosatha.
3 Anene tsono nyumba ya Aroni,
kuti chifundo chake nchosatha.
4 Anene tsono iwo akuopa Yehova,
kuti chifundo chake nchosatha.
5 M’mene ndinasautsika ndinaitanira pa Yehova;
anandiyankha nandiika motakasuka Yehova.
6 Yehova ndi wanga; sindidzaopa;
adzandichitanji munthu?
7 Yehova ndi wanga, mwa iwo akundithandiza;
m’mwemo ndidzaona chofuna ine pa iwo akundida.
8 Kuthawira kwa Yehova nkokoma
koposa kukhulupirira munthu.
9 Kuthawira kwa Yehova nkokoma
koposa kukhulupirira akulu.
10 Amitunduonse adandizinga,
zedi, m’dzina la Yehova ndidzawaduladula.
11 Adandizinga, inde, adandizinga:
Indedi, m’dzina la Yehova ndidzawaduladula.
12 Adandizinga ngati njuchi;
anazima ngati moto waminga;
indedi, m’dzina la Yehova ndidzawaduladula.
13 Kundikankha anandikankha ndikadagwa;
koma Yehova anandithandiza.
14 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;
ndipo anakhala chipulumutso changa.
15 M’mahema a olungama muli liu lakufuula mokondwera
Dzanja lamanja la Yehova ndi la chipulumutso:
16 Dzanja lamanja la Yehova likwezeka,
Dzanja lamanja la Yehova lichita mwamphamvu.
17 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo,
ndipo ndidzafotokozera ntchito za Yehova.
18 Kulanga anandilangadi Yehova:
koma sanandipereke kuimfa ai.
19 Nditsegulireni zipata za chilungamo;
ndidzalowamo, ndidzayamika Yehova.
20 Chipata cha Yehova ndi ichi;
olungama adzalowamo.
21 Ndidzakuyamikani, popeza munandiyankha,
ndipo munakhala chipulumutso changa.
22 Mwala umene omangawo anaukana
wakhala mutu wa pangodya.
23 Ichi chidzera kwa Yehova;
nchodabwitsa ichi pamaso pathu.
24 Tsiku ili ndilo adaliika Yehova;
tidzasekera ndi kukondwera m’mwemo.
25 Tikupemphani, Yehova, tipulumutseni tsopano;
tikupemphani, Yehova, tipindulitseni tsopano.
26 Wodala wakudzayo m’dzina la Yehova;
takudalitsani kochokera m’nyumba ya Yehova.
27 Yehova ndiye Mulungu, amene anatiunikira;
mangani nsembe ndi zingwe, kunyanga za guwa la nsembe.
28 Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani;
ndinu Mulungu wanga, ndidzakukwezani.
29 Yamikani Yehova, pakuti Iye ndiye wabwino,
pakuti chifundo chake nchosatha.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/118-ea1f8e4aa14fcd99c2b772e2e0d4c19c.mp3?version_id=1068—