Categories
MASALIMO

MASALIMO 115

Mulungu ndi wa ulemerero, mafano ndiwo achabe

1 Kwa ife ai, Yehova, kwa ife ai,

koma kwa dzina lanu patsani ulemerero,

chifukwa cha chifundo chanu, ndi choonadi chanu.

2 Aneneranjiamitundu,

Ali kuti Mulungu wao?

3 Koma Mulungu wathu ndiye ali m’mwamba;

achita chilichonse chimkonda.

4 Mafano ao ndiwo asilivandi golide,

ntchito za manja a anthu.

5 Pakamwa ali napo, koma osalankhula;

maso ali nao, koma osapenya;

6 makutu ali nao, koma osamva;

mphuno ali nazo, koma osanunkhiza;

7 manja ali nao, koma osagwira;

mapazi ali nao, koma osayenda;

kapena sanena pammero pao.

8 Adzafanana nao iwo akuwapanga;

ndi onse akuwakhulupirira.

9 Israele, khulupirira Yehova:

Ndiye mthandizi wao ndi chikopa chao.

10 Nyumba ya Aroni, khulupirira Yehova:

Ndiye mthandizi wao, ndi chikopa chao.

11 Inu akuopa Yehova, khulupirirani Yehova;

ndiye mthandizi wao ndi chikopa chao.

12 Yehova watikumbukira; adzatidalitsa:

adzadalitsa nyumba ya Israele;

adzadalitsa nyumba ya Aroni.

13 Adzadalitsa iwo akuopa Yehova,

aang’ono ndi aakulu.

14 Yehova akuonjezereni dalitso,

inu ndi ana anu.

15 Odalitsika inu a kwa Yehova,

wakulenga kumwamba ndi dziko lapansi.

16 Kunena za kumwamba, kumwamba ndiko kwa Yehova;

koma dziko lapansi analipereka kwa ana a anthu.

17 Akufa salemekeza Yehova,

kapena aliyense wakutsikira kuli chete:

18 Koma ife tidzalemekeza Yehova

kuyambira tsopano kufikira nthawi yonse.

Aleluya.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/115-0d615b1f7103a4c1fa3eacfa1fef0728.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *