Mulungu ndi wa ulemerero, mafano ndiwo achabe
1 Kwa ife ai, Yehova, kwa ife ai,
koma kwa dzina lanu patsani ulemerero,
chifukwa cha chifundo chanu, ndi choonadi chanu.
2 Aneneranjiamitundu,
Ali kuti Mulungu wao?
3 Koma Mulungu wathu ndiye ali m’mwamba;
achita chilichonse chimkonda.
4 Mafano ao ndiwo asilivandi golide,
ntchito za manja a anthu.
5 Pakamwa ali napo, koma osalankhula;
maso ali nao, koma osapenya;
6 makutu ali nao, koma osamva;
mphuno ali nazo, koma osanunkhiza;
7 manja ali nao, koma osagwira;
mapazi ali nao, koma osayenda;
kapena sanena pammero pao.
8 Adzafanana nao iwo akuwapanga;
ndi onse akuwakhulupirira.
9 Israele, khulupirira Yehova:
Ndiye mthandizi wao ndi chikopa chao.
10 Nyumba ya Aroni, khulupirira Yehova:
Ndiye mthandizi wao, ndi chikopa chao.
11 Inu akuopa Yehova, khulupirirani Yehova;
ndiye mthandizi wao ndi chikopa chao.
12 Yehova watikumbukira; adzatidalitsa:
adzadalitsa nyumba ya Israele;
adzadalitsa nyumba ya Aroni.
13 Adzadalitsa iwo akuopa Yehova,
aang’ono ndi aakulu.
14 Yehova akuonjezereni dalitso,
inu ndi ana anu.
15 Odalitsika inu a kwa Yehova,
wakulenga kumwamba ndi dziko lapansi.
16 Kunena za kumwamba, kumwamba ndiko kwa Yehova;
koma dziko lapansi analipereka kwa ana a anthu.
17 Akufa salemekeza Yehova,
kapena aliyense wakutsikira kuli chete:
18 Koma ife tidzalemekeza Yehova
kuyambira tsopano kufikira nthawi yonse.
Aleluya.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/115-0d615b1f7103a4c1fa3eacfa1fef0728.mp3?version_id=1068—