Alemekeze Mulungu pa chipulumutso chija cha mu Ejipito
1 M’mene Israele anatuluka ku Ejipito,
nyumba ya Yakobo kwa anthu a chinenedwe chachilendo;
2 Yuda anakhala malo ake oyera, Israele ufumu wake.
3 Nyanjayo inaona, nithawa;
Yordani anabwerera m’mbuyo.
4 Mapiri anatumphatumpha ngati nkhosa zamphongo,
timapiri ngati anaankhosa.
5 Unathawanji nawe, nyanja iwe?
Unabwereranji m’mbuyo, Yordani iwe?
6 Munatumphatumphiranji ngati nkhosa zamphongo, mapiri inu?
Ngati anaankhosa, zitunda inu?
7 Unjenjemere, dziko lapansi iwe, pamaso pa Ambuye,
pamaso pa Mulungu wa Yakobo;
8 amene anasanduliza thanthwe likhale thawale lamadzi,
nsangalabwi ikhale kasupe wamadzi.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/114-5ab6e84572c010674e158936ab27822a.mp3?version_id=1068—