Categories
MASALIMO

MASALIMO 114

Alemekeze Mulungu pa chipulumutso chija cha mu Ejipito

1 M’mene Israele anatuluka ku Ejipito,

nyumba ya Yakobo kwa anthu a chinenedwe chachilendo;

2 Yuda anakhala malo ake oyera, Israele ufumu wake.

3 Nyanjayo inaona, nithawa;

Yordani anabwerera m’mbuyo.

4 Mapiri anatumphatumpha ngati nkhosa zamphongo,

timapiri ngati anaankhosa.

5 Unathawanji nawe, nyanja iwe?

Unabwereranji m’mbuyo, Yordani iwe?

6 Munatumphatumphiranji ngati nkhosa zamphongo, mapiri inu?

Ngati anaankhosa, zitunda inu?

7 Unjenjemere, dziko lapansi iwe, pamaso pa Ambuye,

pamaso pa Mulungu wa Yakobo;

8 amene anasanduliza thanthwe likhale thawale lamadzi,

nsangalabwi ikhale kasupe wamadzi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/114-5ab6e84572c010674e158936ab27822a.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *