Categories
MASALIMO

MASALIMO 113

Anthu onse alemekeze dzina la Mulungu wothandiza aumphawi

1 Aleluya;

Lemekezani, inu atumiki a Yehova;

lemekezani dzina la Yehova.

2 Lodala dzina la Yehova Kuyambira tsopano kufikira kosatha.

3 Chitulukire dzuwa kufikira kulowa kwake

lilemekezedwe dzina la Yehova.

4 Yehova akwezeka pamwamba paamitunduonse,

ulemerero wake pamwambamwamba.

5 Akunga Yehova Mulungu wathu ndani?

Amene akhala pamwamba patali,

6 nadzichepetsa apenye

zam’mwamba ndi za padziko lapansi.

7 Amene autsa wosauka kumchotsa kufumbi,

nakweza waumphawi kumchotsa kudzala.

8 Kuti amkhalitse pamodzi ndi akulu,

pamodzi ndi akulu a anthu ake.

9 Asungitsa nyumba mkazi wosaona mwana,

akhale mai wokondwera ndi ana.

Aleluya.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/113-80e0287586e593a9476072f8b40eebd9.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *