Anthu onse alemekeze dzina la Mulungu wothandiza aumphawi
1 Aleluya;
Lemekezani, inu atumiki a Yehova;
lemekezani dzina la Yehova.
2 Lodala dzina la Yehova Kuyambira tsopano kufikira kosatha.
3 Chitulukire dzuwa kufikira kulowa kwake
lilemekezedwe dzina la Yehova.
4 Yehova akwezeka pamwamba paamitunduonse,
ulemerero wake pamwambamwamba.
5 Akunga Yehova Mulungu wathu ndani?
Amene akhala pamwamba patali,
6 nadzichepetsa apenye
zam’mwamba ndi za padziko lapansi.
7 Amene autsa wosauka kumchotsa kufumbi,
nakweza waumphawi kumchotsa kudzala.
8 Kuti amkhalitse pamodzi ndi akulu,
pamodzi ndi akulu a anthu ake.
9 Asungitsa nyumba mkazi wosaona mwana,
akhale mai wokondwera ndi ana.
Aleluya.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/113-80e0287586e593a9476072f8b40eebd9.mp3?version_id=1068—