Adalitsidwa akuopa Mulungu
1 Aleluya.
Wodala munthu wakuopa Yehova,
wakukondwera kwambiri ndi malamulo ake.
2 Mbeu yake idzakhala yamphamvu padziko lapansi;
mbadwo wa oongoka mtima udzadalitsidwa.
3 M’nyumba mwake mudzakhala akatundu ndi chuma:
Ndi chilungamo chake chikhala chikhalire.
4 Kuunika kutulukira oongoka mtima mumdima;
Iye ndiye wachisomo, ndi wansoni ndi wolungama.
5 Wodala munthu wakuchitira chifundo, nakongoletsa;
adzalimbika nao mlandu wake poweruzidwa.
6 Popeza sadzagwedezeka nthawi zonse;
wolungama adzakumbukika ku nthawi yosatha.
7 Sadzaopa mbiri yoipa;
mtima wake ngwokhazikika, wokhulupirira Yehova.
8 Mtima wake ngwochirikizika, sadzachita mantha,
kufikira ataona chofuna iye pa iwo omsautsa.
9 Anagawagawa, anapatsa aumphawi;
chilungamo chake chikhalitsa kosatha;
nyanga yake idzakwezeka ndi ulemu.
10 Woipa adzaziona, nadzapsa mtima;
adzakukuta mano, nadzasungunuka;
chokhumba oipa chidzatayika.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/112-54499c8107a4ce09f7f943fb8a67cffa.mp3?version_id=1068—