Categories
MASALIMO

MASALIMO 112

Adalitsidwa akuopa Mulungu

1 Aleluya.

Wodala munthu wakuopa Yehova,

wakukondwera kwambiri ndi malamulo ake.

2 Mbeu yake idzakhala yamphamvu padziko lapansi;

mbadwo wa oongoka mtima udzadalitsidwa.

3 M’nyumba mwake mudzakhala akatundu ndi chuma:

Ndi chilungamo chake chikhala chikhalire.

4 Kuunika kutulukira oongoka mtima mumdima;

Iye ndiye wachisomo, ndi wansoni ndi wolungama.

5 Wodala munthu wakuchitira chifundo, nakongoletsa;

adzalimbika nao mlandu wake poweruzidwa.

6 Popeza sadzagwedezeka nthawi zonse;

wolungama adzakumbukika ku nthawi yosatha.

7 Sadzaopa mbiri yoipa;

mtima wake ngwokhazikika, wokhulupirira Yehova.

8 Mtima wake ngwochirikizika, sadzachita mantha,

kufikira ataona chofuna iye pa iwo omsautsa.

9 Anagawagawa, anapatsa aumphawi;

chilungamo chake chikhalitsa kosatha;

nyanga yake idzakwezeka ndi ulemu.

10 Woipa adzaziona, nadzapsa mtima;

adzakukuta mano, nadzasungunuka;

chokhumba oipa chidzatayika.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/112-54499c8107a4ce09f7f943fb8a67cffa.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *