Alemekeza Mulungu pa ntchito zao zazikulu zokoma
1 Aleluya.
Ndidzayamika Yehova ndi mtima wonse,
mu upo wa oongoka mtima, ndi mumsonkhano.
2 Ntchito za Yehova nzazikulu,
zofunika ndi onse akukondwera nazo.
3 Chochita Iye ncha ulemu, ndi ukulu:
Ndi chilungamo chake chikhalitsa kosatha.
4 Anachita chokumbukitsa zodabwitsa zake;
Yehova ndiye wachisomo ndi nsoni zokoma.
5 Anapatsa akumuopa Iye chakudya;
adzakumbukirachipanganochake kosatha.
6 Anaonetsera anthu ake mphamvu ya ntchito zake,
pakuwapatsa cholowa chaamitundu.
7 Ntchito za manja ake ndizo choonadi ndi chiweruzo;
malangizo ake onse ndiwo okhulupirika.
8 Achirikizika kunthawi za nthawi,
achitika m’choonadi ndi chilunjiko.
9 Anatumizira anthu ake chipulumutso;
analamulira chipangano chake kosatha;
dzina lake ndilo loyera ndi loopedwa.
10 Kumuopa Yehova ndiko chiyambi cha nzeru;
onse akuchita chotero ali nacho chidziwitso chokoma;
chilemekezo chake chikhalitsa kosatha.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/111-48a698421ca28f8091fe9ff011fd8829.mp3?version_id=1068—