Categories
MASALIMO

MASALIMO 111

Alemekeza Mulungu pa ntchito zao zazikulu zokoma

1 Aleluya.

Ndidzayamika Yehova ndi mtima wonse,

mu upo wa oongoka mtima, ndi mumsonkhano.

2 Ntchito za Yehova nzazikulu,

zofunika ndi onse akukondwera nazo.

3 Chochita Iye ncha ulemu, ndi ukulu:

Ndi chilungamo chake chikhalitsa kosatha.

4 Anachita chokumbukitsa zodabwitsa zake;

Yehova ndiye wachisomo ndi nsoni zokoma.

5 Anapatsa akumuopa Iye chakudya;

adzakumbukirachipanganochake kosatha.

6 Anaonetsera anthu ake mphamvu ya ntchito zake,

pakuwapatsa cholowa chaamitundu.

7 Ntchito za manja ake ndizo choonadi ndi chiweruzo;

malangizo ake onse ndiwo okhulupirika.

8 Achirikizika kunthawi za nthawi,

achitika m’choonadi ndi chilunjiko.

9 Anatumizira anthu ake chipulumutso;

analamulira chipangano chake kosatha;

dzina lake ndilo loyera ndi loopedwa.

10 Kumuopa Yehova ndiko chiyambi cha nzeru;

onse akuchita chotero ali nacho chidziwitso chokoma;

chilemekezo chake chikhalitsa kosatha.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/111-48a698421ca28f8091fe9ff011fd8829.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *