Ufumu wa Ambuye
Salimo la Davide.
1 Yehova ananena kwa Ambuye wanga,
Khalani padzanja lamanja langa,
kufikira nditaika adani anu chopondapo mapazi anu.
2 Yehova adzatumiza ndodo ya mphamvu yanu kuchokera kuZiyoni;
chitani ufumu pakati pa adani anu.
3 Anthu anu adzadzipereka eni ake tsiku la chamuna chanu:
M’moyera mokometsetsa, mobadwira matanda kucha,
muli nao mame a ubwana wanu.
4 Yehova walumbira, ndipo sadzasintha,
Inu ndinu wansembe kosatha
monga mwa chilongosoko chaMelkizedeki.
5 Ambuye padzanja lamanja lako
adzaphwanya mafumu tsiku la mkwiyo wake.
6 Adzaweruza mwaamitundu,
adzadzaza dziko ndi mitembo;
adzaphwanya mitu m’maiko ambiri.
7 Adzamwa kumtsinje wa panjira;
chifukwa chake adzaweramutsa mutu wake.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/110-cb1ea9992b1b11c76287ea4ef90ccbb9.mp3?version_id=1068—