Categories
MASALIMO

MASALIMO 110

Ufumu wa Ambuye

Salimo la Davide.

1 Yehova ananena kwa Ambuye wanga,

Khalani padzanja lamanja langa,

kufikira nditaika adani anu chopondapo mapazi anu.

2 Yehova adzatumiza ndodo ya mphamvu yanu kuchokera kuZiyoni;

chitani ufumu pakati pa adani anu.

3 Anthu anu adzadzipereka eni ake tsiku la chamuna chanu:

M’moyera mokometsetsa, mobadwira matanda kucha,

muli nao mame a ubwana wanu.

4 Yehova walumbira, ndipo sadzasintha,

Inu ndinu wansembe kosatha

monga mwa chilongosoko chaMelkizedeki.

5 Ambuye padzanja lamanja lako

adzaphwanya mafumu tsiku la mkwiyo wake.

6 Adzaweruza mwaamitundu,

adzadzaza dziko ndi mitembo;

adzaphwanya mitu m’maiko ambiri.

7 Adzamwa kumtsinje wa panjira;

chifukwa chake adzaweramutsa mutu wake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/110-cb1ea9992b1b11c76287ea4ef90ccbb9.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *