Categories
MASALIMO

MASALIMO 11

Yehova asunga anthu ake nalanga oipa

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide.

1 Ndakhulupirira Yehova,

mutani nkunena kwa moyo wanga,

Thawirani kuphiri lanu ngati mbalame?

2 Pakuti, onani, oipa akoka uta,

apiringidza muvi wao pansinga,

kuwaponyera mumdima oongoka mtima.

3 Akapasuka maziko,

wolungama angachitenji?

4 Yehova ali mu Kachisi wake woyera,

Yehova, mpando wachifumu wake uli mu Mwamba;

apenyerera ndi maso ake, ayesa ana a anthu ndi zikope zake.

5 Yehova ayesa wolungama mtima,

koma moyo wake umuda woipa ndi iye wakukonda chiwawa.

6 Adzagwetsa pwatapwata misampha pa oipa;

moto ndi miyala yasulufure,

ndi mphepo yoopsa zidzawagawikira m’chikho chao.

7 Pakuti Yehova ndiye wolungama; akonda zolungama;

woongoka mtima adzapenya nkhope yake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/11-6a0cc3d8a7d5d581b3105676a8e68595.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *