Yehova asunga anthu ake nalanga oipa
Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide.
1 Ndakhulupirira Yehova,
mutani nkunena kwa moyo wanga,
Thawirani kuphiri lanu ngati mbalame?
2 Pakuti, onani, oipa akoka uta,
apiringidza muvi wao pansinga,
kuwaponyera mumdima oongoka mtima.
3 Akapasuka maziko,
wolungama angachitenji?
4 Yehova ali mu Kachisi wake woyera,
Yehova, mpando wachifumu wake uli mu Mwamba;
apenyerera ndi maso ake, ayesa ana a anthu ndi zikope zake.
5 Yehova ayesa wolungama mtima,
koma moyo wake umuda woipa ndi iye wakukonda chiwawa.
6 Adzagwetsa pwatapwata misampha pa oipa;
moto ndi miyala yasulufure,
ndi mphepo yoopsa zidzawagawikira m’chikho chao.
7 Pakuti Yehova ndiye wolungama; akonda zolungama;
woongoka mtima adzapenya nkhope yake.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/11-6a0cc3d8a7d5d581b3105676a8e68595.mp3?version_id=1068—