Categories
MASALIMO

MASALIMO 108

Davide aimbira Mulungu womgonjetsera adani

Nyimbo. Salimo la Davide.

1 Wakhazikika mtima wanga, Mulungu;

ndidzaimba, inde ndidzaimba zolemekeza, ndiko ulemerero wanga.

2 Galamukani, chisakasa ndi zeze;

ndidzauka ndekha mamawa.

3 Ndidzakuyamikani mwa mitundu ya anthu, Yehova:

ndipo ndidzaimba zakukulemekezani mwa anthu.

4 Pakuti chifundo chanu nchachikulu kupitirira kumwamba,

ndi choonadi chanu kufikira mitambo.

5 Kwezekani pamwamba pa thambo, Mulungu;

ndi ulemerero wanu pamwamba padziko lonse lapansi,

6 kuti okondedwa anu alanditsidwe,

pulumutsani ndi dzanja lanu lamanja ndipo mutivomereze.

7 Mulungu analankhula m’chiyero chake; ndidzakondwerera:

ndidzagawa Sekemu; ndidzayesa muyeso chigwa cha Sukoti.

8 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanga;

ndi Efuremu ndiye mphamvu ya mutu wanga;

Yuda ndiye wolamulira wanga.

9 Mowabu ndiye mkhate wanga;

pa Edomu ndidzaponya nsapato yanga;

ndidzafuulira Filistiya.

10 Adzandifikitsa ndani m’mzinda wa m’linga?

Adzanditsogolera ndani ku Edomu?

11 Si ndinu Mulungu, amene mwatitaya

osatuluka nao magulu athu?

12 Tithandizeni mumsauko;

pakuti chipulumutso cha munthu ndi chabe.

13 Mwa Mulungu tidzachita molimbika mtima:

Ndipo Iye adzapondereza otisautsa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/108-b23f6266034aa4eada30b38fe6a206bb.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *