Alemekeze Yehova pa chifundo chake chachikulu
Salimo la Davide.
1 Lemekeza Yehova, moyo wanga;
ndi zonse za m’kati mwanga zilemekeze dzina lake loyera.
2 Lemekeza Yehova, moyo wanga,
ndi kusaiwala zokoma zake zonse atichitirazi:
3 Amene akhululukira mphulupulu zako zonse;
nachiritsa nthenda zako zonse;
4 amene aombola moyo wako ungaonongeke;
nakuveka korona wa chifundo ndi nsoni zokoma:
5 Amene akhutitsa m’kamwa mwako ndi zabwino;
nabweza ubwana wako unge mphungu.
6 Yehova achitira onse osautsidwa
chilungamo ndi chiweruzo.
7 Analangiza Mose njira zake,
ndi ana a Israele machitidwe ake.
8 Yehova ndiye wa nsoni zokoma ndi wachisomo,
wosakwiya msanga, ndi wa chifundo chochuluka.
9 Sadzatsutsana nao nthawi zonse;
ndipo sadzasunga mkwiyo wake kosatha.
10 Sanatichitira monga mwa zolakwa zathu,
kapena kutibwezera monga mwa mphulupulu zathu.
11 Pakuti monga m’mwamba mutalikira ndi dziko lapansi,
motero chifundo chake chikulira iwo akumuopa Iye.
12 Monga kum’mawa kutanimpha ndi kumadzulo,
momwemo anatisiyanitsira kutali zolakwa zathu.
13 Monga atate achitira ana ake chifundo,
Yehova achitira chifundo iwo akumuopa Iye.
14 Popeza adziwa mapangidwe athu;
akumbukira kuti ife ndife fumbi.
15 Koma munthu, masiku ake akunga udzu;
aphuka monga duwa lakuthengo.
16 Pakuti mphepo ikapitapo pakhala palibe:
Ndi malo ake salidziwanso.
17 Koma chifundo cha Yehova ndicho choyambira nthawi yosayamba
kufikira nthawi yosatha kwa iwo akumuopa Iye,
ndi chilungamo chake kufikira kwa ana a ana;
18 kwa iwo akusungachipanganochake,
ndi kwa iwo akukumbukira malangizo ake kuwachita.
19 Yehova anakhazika mpando wachifumu wake Kumwamba;
ndi ufumu wake uchita mphamvu ponsepo.
20 Lemekezani Yehova, inuangeloake;
a mphamvu zolimba, akuchita mau ake,
akumvera liu la mau ake.
21 Lemekezani Yehova, inu makamu ake onse;
inu atumiki ake akuchita chomkondweretsa Iye.
22 Lemekezani Yehova, inu, ntchito zake zonse,
ponseponse pali ufumu wake:
Lemekeza Yehova, moyo wanga iwe.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/103-bb77833f2fd6c75b7d2f1ad734162366.mp3?version_id=1068—