Categories
MASALIMO

MASALIMO 101

Davide akuti adzasamala okhulupirika nadzachotsa oipa

Salimo la Davide.

1 Ndidzaimba zachifundo ndi chiweruzo;

ndidzaimba zakukulemekezani Inu, Yehova.

2 Ndidzachita mwanzeru m’njira yangwiro;

mudzandidzera liti?

Ndidzayenda m’nyumba mwanu ndi mtima wangwiro.

3 Sindidzaika chinthu choipa pamaso panga;

chochita iwo akupatuka padera chindiipira;

sichidzandimamatira.

4 Mtima wopulukira udzandichokera;

sindidzadziwana naye woipa.

5 Wakuneneza mnzake m’tseri ndidzamdula;

wa maso odzikuza ndi mtima wodzitama sindidzamlola.

6 Maso anga ayang’ana okhulupirika m’dziko, kuti akhale ndi Ine;

iye amene ayenda m’njira yangwiro, iyeyu adzanditumikira Ine.

7 Wakuchita chinyengo sadzakhala m’kati mwa nyumba yanga;

wakunena mabodza sadzakhazikika pamaso panga.

8 Mamawa onse ndidzadula oipa onse a m’dziko;

kuduliratu onse akuchita zopanda pake kumzinda wa Yehova.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/101-c79d9d75fa245d4b3f9ed3cd86427ff4.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *