Olengedwa ndi Mulungu amlemekeze
Salimo la Chiyamiko.
1 Fuulirani kwa Yehova, inu, dziko lonse lapansi.
2 Tumikirani Yehova ndi chikondwerero:
Idzani pamaso pake ndi kumuimbira mokondwera.
3 Dziwani kuti Yehova ndiye Mulungu;
Iyeyu anatilenga, ndipo ife ndife ake;
ndife anthu ake ndi nkhosa zapabusa pake.
4 Lowani kuzipata zake ndi chiyamiko,
ndi kumabwalo ake ndi chilemekezo:
Myamikeni; lilemekezeni dzina lake.
5 Pakuti Yehova ndiye wabwino;
chifundo chake chimanka muyaya;
ndi chikhulupiriko chake ku mibadwomibadwo.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/100-aa94a0038194128acb99efca962c0162.mp3?version_id=1068—