Categories
MASALIMO

MASALIMO 100

Olengedwa ndi Mulungu amlemekeze

Salimo la Chiyamiko.

1 Fuulirani kwa Yehova, inu, dziko lonse lapansi.

2 Tumikirani Yehova ndi chikondwerero:

Idzani pamaso pake ndi kumuimbira mokondwera.

3 Dziwani kuti Yehova ndiye Mulungu;

Iyeyu anatilenga, ndipo ife ndife ake;

ndife anthu ake ndi nkhosa zapabusa pake.

4 Lowani kuzipata zake ndi chiyamiko,

ndi kumabwalo ake ndi chilemekezo:

Myamikeni; lilemekezeni dzina lake.

5 Pakuti Yehova ndiye wabwino;

chifundo chake chimanka muyaya;

ndi chikhulupiriko chake ku mibadwomibadwo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/100-aa94a0038194128acb99efca962c0162.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *