Athamangira Mulungu pothawa adani omtsata
1 Muimiranji patali, Yehova?
Mubisaliranji m’nyengo za nsautso?
2 Podzikuza woipa apsereza waumphawi;
agwe m’chiwembu anapanganacho.
3 Pakuti woipa adzitamira chifuniro cha moyo wake,
adalitsa wosirira, koma anyoza Yehova.
4 Woipa, monga mwa kudzikuza kwa nkhope yake, akuti, Sadzafunsira.
Malingaliro ake onse akuti, Palibe Mulungu.
5 Mayendedwe ake alimbika nthawi zonse;
maweruzo anu ali pamwamba posaona iye;
adani ake onse awanyodola.
6 Ati mumtima mwake, Sindidzagwedezeka ine;
ku mibadwomibadwo osagwa m’tsoka ine.
7 M’kamwa mwake mwadzala kutemberera
ndi manyengo ndi kuchenjerera;
pansi pa lilime lake pali chivutitso chopanda pake.
8 Akhala m’molalira midzi;
mobisalamo akupha munthu wosachimwa.
Ambisira waumphawi nkhope yake.
9 Alalira monga mkango m’ngaka mwake;
alalira kugwira wozunzika,
agwira wozunzika, pakumkola mu ukonde mwake.
10 Aunthama, nawerama,
ndipo aumphawi agwa m’zala zake.
11 Anena m’mtima mwake, Mulungu waiwala;
wabisa nkhope yake; sapenya nthawi zonse.
12 Ukani, Yehova; samulani dzanja lanu, Mulungu;
musaiwale ozunzika.
13 Woipa anyozeranji Mulungu,
anena m’mtima mwake, Simudzafunsira?
14 Mwapenya; pakuti mumayang’anira chivutitso
ndi chisoni kuti achipereke m’manja mwanu;
waumphawi adzipereka kwa Inu;
wamasiye mumakhala mthandizi wake.
15 Thyolani mkono wa woipa;
ndipo wochimwa, mutsate choipa chake
kufikira simuchipezanso china.
16 Yehova ndiye Mfumu kunthawi yamuyaya;
aonongekaamitundum’dziko lake.
17 Yehova, mwamva chikhumbo cha ozunzika,
mudzakhazikitsa mtima wao, mudzatchereza khutu lanu;
18 kuti muweruze mlandu wa amasiye ndi wokhalira mphanthi,
kuti munthu wa padziko lapansi angaonjeze kuopsa.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/10-4363149da873ad6239f11877cd226247.mp3?version_id=1068—