Categories
MASALIMO

MASALIMO 1

Kusiyana pakati pa olungama ndi oipa

1 Wodala munthuyo wosayenda mu uphungu wa oipa,

kapena wosaimirira m’njira ya ochimwa,

kapena wosakhala pansi pa bwalo la onyoza.

2 Komatu m’chilamulo cha Yehova muli chikondwerero chake;

ndipo m’chilamulo chake amalingirira usana ndi usiku.

3 Ndiye akunga mtengo wooka pa mitsinje ya madzi;

wakupatsa chipatso chake pa nyengo yake,

tsamba lake lomwe losafota;

ndipo zonse azichita apindula nazo.

4 Oipa satero ai;

koma akunga mungu wouluka ndi mphepo.

5 Chifukwa chake oipa sadzaimirira pa mlanduwo,

kapena ochimwa mu msonkhano wa olungama.

6 Pakuti Yehova adziwa mayendedwe a olungama;

koma mayendedwe a oipa adzatayika.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/1-7cc95113bd363644c1c5933efc45eb76.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *