Kusiyana pakati pa olungama ndi oipa
1 Wodala munthuyo wosayenda mu uphungu wa oipa,
kapena wosaimirira m’njira ya ochimwa,
kapena wosakhala pansi pa bwalo la onyoza.
2 Komatu m’chilamulo cha Yehova muli chikondwerero chake;
ndipo m’chilamulo chake amalingirira usana ndi usiku.
3 Ndiye akunga mtengo wooka pa mitsinje ya madzi;
wakupatsa chipatso chake pa nyengo yake,
tsamba lake lomwe losafota;
ndipo zonse azichita apindula nazo.
4 Oipa satero ai;
koma akunga mungu wouluka ndi mphepo.
5 Chifukwa chake oipa sadzaimirira pa mlanduwo,
kapena ochimwa mu msonkhano wa olungama.
6 Pakuti Yehova adziwa mayendedwe a olungama;
koma mayendedwe a oipa adzatayika.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/1-7cc95113bd363644c1c5933efc45eb76.mp3?version_id=1068—