Categories
MARKO

MARKO 2

Achiritsa wodwala manjenje

1 Ndipo polowanso Iye mu Kapernao atapita masiku ena, kunamveka kuti ali m’nyumba.

2 Ndipo ambiri anaunjikana, kotero kuti anasowa malo, ngakhale pakhomo pomwe; ndipo analankhula nao mau.

3 Ndipo anadza kwa Iye otenga munthu wodwala manjenje, wonyamulidwa ndi anthu anai.

4 Ndipo pamene sanakhoze kufika kuli Iye, chifukwa cha khamu la anthu, anasasula tsindwi pokhala Iye; ndipo pamene anatha kuliboola, anatsitsa mphasa m’mene alinkugonamo wodwala manjenjeyo.

5 Ndipo Yesu pakuona chikhulupiriro chao ananena ndi wodwala manjenje, Mwana, machimo ako akhululukidwa.

6 Koma anakhalapo ena a alembi akuganizira mumtima mwao,

7 Munthu amene atero bwanji? Achita mwano; akhoza ndani kukhululukira machimo, koma mmodzi, ndiye Mulungu?

8 Ndipo pomwepo Yesu pozindikira mumtima mwake kuti alikuganizira chomwecho mwa iwo okha, ananena nao, Muganiza bwanji zinthu izi m’mitima yanu?

9 Chapafupi nchiti, kuuza wodwala manjenje kuti, Machimo ako akhululukidwa; kapena kuti, Nyamuka, senza mphasa yako, nuyende?

10 Koma kuti mudziwe kutiMwana wa Munthuali mwini ulamuliro wakukhululukira machimo padziko lapansi (ananena ndi wodwala manjenje),

11 Ndikuuza iwe, Nyamuka, senza mphasa yako, numuke kwanu.

12 Ndipo ananyamuka iye pomwepo, nasenza mphasa, natuluka pamaso pa iwo onse; kotero kuti anadabwa onse, nalemekeza Mulungu, nanena kuti, Zotere sitinazione ndi kale lonse.

Yesu aitana Levi

13 Ndipo anatulukanso kunka m’mbali mwa nyanja; ndipo linadza kwa Iye khamu lonse la anthu, ndipo anawaphunzitsa.

14 Ndipo pakumuka, naona Levi mwana wa Alifeyo alikukhala polandirira msonkho, ndipo ananena naye, Tsata Ine.

15 Ndipo ananyamuka namtsata Iye. Ndipo kunali kuti anakhala pakudya m’nyumba mwake, ndipoamisonkhondi ochimwa ambiri anakhala pansi pamodzi ndi Yesu ndiophunziraake, pakuti anali ambiri, ndipo anamtsata Iye.

16 Ndipo alembi a kwaAfarisi, pakuona kuti alinkudya nao ochimwa ndi amisonkho, ananena ndi ophunzira ake, Uyu akudya ndi kumwa nao amisonkho ndi ochimwa.

17 Ndipo pamene Yesu anamva ichi, ananena nao, Akulimba safuna sing’anga, koma odwala ndiwo; sindinadza kudzaitana olungama, koma ochimwa.

Kudzikana kudya

18 Ndipo ophunzira a Yohane ndi Afarisi analinkusala kudya; ndipo anadza, nanena ndi Iye, Bwanji asala kudya ophunzira a Yohane, ndi ophunzira a Afarisi, koma ophunzira anu sasala kudya?

19 Ndipo Yesu ananena nao, Kodi akhoza kusala kudya anyamata a ukwati pamene mkwati ali pamodzi nao? Pokhala ali naye mkwati pamodzi ndi iwo sangathe kusala.

20 Koma adzadza masiku, pamene mkwati adzachotsedwa kwa iwo, ndipo pamenepo adzasala kudya tsiku lomwelo.

21 Palibe munthu asokerera chigamba cha nsalu yaiwisi pa chofunda chakale; pena chimene choti chidzakonza chizomolapo, chatsopanocho chizomoka pa chakalecho, ndipo chiboo chikulapo.

22 Ndipo palibe munthu amatsanulira vinyo watsopano m’matumba akale: pena vinyo adzaphulitsa matumba, ndipo aonongeka vinyo, ndi matumba omwe: koma vinyo watsopano amatsanulira m’matumba atsopano.

Yesu mwini Sabata

23 Ndipo kunali kuti anapita Iye pakati pa minda tsiku laSabata; ndipo ophunzira ake poyenda anayamba kubudula ngala za dzinthu.

24 Ndipo Afarisi ananena ndi Iye, Taona, achitiranji chosaloleka kuchitika tsiku la Sabata?

25 Ndipo ananena nao, Simunawerenge konse chimene anachichita Davide, pamene adasowa, namva njala, iye ndi iwo amene anali pamodzi naye?

26 Kuti analowa m’nyumba ya Mulungu masiku a Abiyatara, mkulu wa ansembe, ndipo anadya mikate yoonetsera, yosaloleka kudya ena, koma ansembe okha, ndipo anawapatsanso iwo amene anali naye?

27 Ndipo ananena nao, Sabata linaikidwa chifukwa cha munthu, si munthu chifukwa cha Sabata;

28 motero Mwana wa Munthu ali mwini tsiku la Sabata lomwe.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MRK/2-ffab84990ed7d75525d03ade6d2850d2.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *