Categories
MARKO

MARKO 11

Yesu alowa mu Yerusalemu alikukhala pabulu

1 Ndipo pamene iwo anayandikira kuYerusalemu, ku Betefage ndi Betaniya, paphiri la Azitona, anatuma awiri aophunziraake,

2 nanena nao, Mukani, lowani m’mudzi wapandunji ndi inu; ndipo pomwepo pakulowamo mudzapeza mwana wa bulu womangidwa, amene palibe munthu anakhalapo kale lonse; mmasuleni, ndipo mubwere naye.

3 Ndipo munthu akati kwa inu, Mutero bwanji? Katini, Ambuye amfuna iye; ndipo pomwepo adzamtumiza kuno.

4 Ndipo anachoka, napeza mwana wa bulu womangidwa pakhomo, pabwalo m’khwalala, nammasula iye.

5 Ndipo ena akuima kumeneko ananena nao, Muchita chiyani ndi kumasula mwana wa bulu?

6 Ndipo anati kwa iwo monga momwe ananena Yesu: ndipo anawalola iwo apite naye.

7 Ndipo anabwera naye mwana wa bulu kwa Yesu, naika zovala zao pa iye, ndipo Iye anakhala pamenepo.

8 Ndimo ambiri anayala zovala zao panjira; ndi ena zitsamba, anazidula m’minda.

9 Ndipo akutsogolera, ndi iwo akutsata, anafuula, Hosana; Wolemekezeka Iye wakudza m’dzina la Ambuye:

10 Wolemekezeka Ufumu ulinkudza, wa atate wathu Davide; Hosana mu Kumwambamwamba.

11 Ndipo Iye analowa mu Yerusalemu, mu Kachisi; ndipo m’mene anaunguza zinthu zonse, popeza ndi madzulo, anatuluka kupita ku Betaniya pamodzi ndi khumi ndi awiriwo.

Yesu atemberera mkuyu

12 Ndipo m’mawa mwake, atatuluka ku Betaniya, Iye anamva njala.

13 Ndipo anaona mkuyu kutali, uli ndi masamba; ndipo anadza Iye, kuti kapena akapezapo kanthu: ndipo m’mene anafikako anapeza palibe kanthu koma masamba okha; pakuti siinali nyengo yake ya nkhuyu.

14 Ndipo anayankha nanena ndi uwo, Munthu sadzadyanso zipatso zako nthawi zonse. Ndipo ophunzira ake anamva.

Yesu atulutsa amalonda mu Kachisi

15 Ndipo anafika iwo ku Yerusalemu; ndipo Iye analowa mu Kachisi, nayamba kutulutsa akugulitsa ndi akugula malonda mu Kachisimo, nagubuduza magome a osinthana ndalama, ndi mipando ya ogulitsa nkhunda;

16 ndipo sanalole munthu aliyense kunyamula chotengera kupyola pakati pa Kachisi.

17 Ndipo anaphunzitsa, nanena nao, Sichilembedwa kodi, Nyumba yanga idzatchedwa nyumba yakupempheramo anthu a mitundu yonse? Koma inu mwaiyesa phanga la achifwamba.

18 Ndipo ansembe aakulu ndi alembi anamva, nafunafuna momuonongera Iye; pakuti anamuopa, chifukwa khamu lonse la anthu linazizwa ndi chiphunzitso chake.

19 Ndipo masiku onse madzulo anatuluka Iye m’mzinda.

Mkuyu wouma

20 Ndipo m’mene anapitapo m’mawa mwake, anaona kuti mkuyu uja unafota, kuyambira kumizu.

21 Ndipo Petro anakumbukira, nanena naye,Rabi, onani, wafota mkuyuwo munautemberera.

22 Ndipo Yesu anayankha nanena nao, Khulupirirani Mulungu.

23 Ndithu ndinena ndi inu, kuti, Munthu aliyense akanena ndi phiri ili, Tanyamulidwa, nuponyedwe m’nyanja; wosakayika mumtima mwake, koma adzakhulupirira kuti chimene achinena chichitidwa, adzakhala nacho.

24 Chifukwa chake ndinena ndi inu, Zinthu zilizonse mukazipemphera ndi kuzipempha, khulupirirani kuti mwazilandira, ndipo mudzakhala nazo.

25 Ndipo pamene muimirira ndi kupemphera, khululukirani, ngati munthu wakulakwirani kanthu; kuti Atate wanunso ali Kumwamba akhululukire inu zolakwa zanu.

Ubatizo wa Yohane

27 Ndipo iwo anadzanso ku Yerusalemu; ndipo m’mene Iye anali kuyenda mu Kachisi, anafika kwa Iye ansembe aakulu, ndi alembi ndi akulu;

28 nanena naye, Izi muzichita ndi ulamuliro wotani? Kapena anakupatsani ndani ulamuliro uwu wakuchita izi?

29 Ndipo Yesu anati kwa iwo, Ndikufunsani mau amodzi, mundiyankhe Ine, ndipo ndidzakuuzani ulamuliro umene ndichita nao zinthu zimenezi.

30 Ubatizo wa Yohane uchokera Kumwamba kodi, kapena kwa anthu? Mundiyankhe.

31 Ndipo anatsutsana mwa iwo okha, nanena, Tikati, Kumwamba; adzanena Iye, Ndipo simunakhulupirire iye bwanji?

32 Koma tikati, Kwa anthu, anaopa anthuwo; pakuti onse anamuyesa Yohanemnenerindithu.

33 Ndipo iwo anamyankha Yesu, ananena nao, Inenso sindikuuzani ulamuliro umene ndichita nao zinthu zimenezi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MRK/11-fb491d5d1e8734a2a6fb421b36b4085d.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *