Categories
MALIRO

MALIRO 4

Tsoka la anthu Ayuda

1 Ha! Golide wagugadi; golide woona woposa wasandulika;

miyala ya malo opatulika yakhuthulidwa

pa malekezero a makwalala onse.

2 Ana aZiyonia mtengo wapatali,

olingana ndi golide woyengetsa,

angoyesedwa ngati mbiya zadothi zozipanga manja a woumba.

3 Angakhale ankhandwe amapatsa bere, nayamwitsa ana ao;

koma mwana wamkazi wa anthu a mtundu wanga

wasanduka wankhanza,

ngati nthiwatiwa za m’chipululu.

4 Lilime la mwana woyamwa limamatira

kumalakalaka kwake ndi ludzu;

ana aang’ono apempha mkate koma palibe wakuwanyemera.

5 Omwe anadya zolongosoka angosiyidwa m’makwalala;

omwe analeredwa navekedwa mlangali afungatira madzala.

6 Pakuti mphulupulu ya mwana wamkazi wa anthu a mtundu wanga,

ikula koposa tchimo la Sodomu,

umene unapasuka m’kamphindi, anthu osauchitira kanthu.

7 Omveka ake anakonzeka

koposa chipale chofewa, nayera koposa mkaka,

matupi ao anafiira koposa timiyala toti psu;

maonekedwe ao ananga a safiro wa mtengo wapatali.

8 Maonekedwe ao ada koposa makala,

sazindikirika m’makwalala;

khungu lao limamatira pa mafupa ao,

lakhwinyata, lasanduka ngati ndodo.

9 Ophedwa ndi lupanga amva bwino

kupambana ophedwa ndi njala;

pakuti amenewa angokwalika napyozedwa,

posowa zipatso za m’munda.

10 Manja a akazi achisoni anaphika ana aoao;

anali chakudya chao poonongeka

mwana wamkazi wa anthu a mtundu wanga.

11 Yehova wakwaniritsa kuzaza kwake, watsanulira ukali wake;

anayatsa moto mu Ziyoni, unanyambita maziko ake.

12 Mafumu a dziko lapansi sanakhulupirire,

ngakhale onse okhala kunja kuno,

kuti adani ndi amaliwongo adzalowadi m’zipata zaYerusalemu.

13 Ndicho chifukwa cha machimo a aneneri

ndi mphulupulu za ansembe ake,

amene anakhetsa mwazi wa olungama pakati pake.

14 Asochera m’makwalala ngati akhungu,

aipsidwa ndi mwazi;

anthu sangakhudze zovala zao.

15 Amafuula kwa iwo, Chokani, osakonzeka inu,

chokani, chokani, musakhudze kanthu.

Pothawa iwo ndi kusochera,

anthu anati kwaamitundu,

Sadzagoneranso kuno.

16 Mkwiyo wa Yehova unawalekanitsa, sadzawasamaliranso;

iwo sanalemekeze ansembe, sanakomere mtima akulu.

17 Maso athu athedwa, tikali ndi moyo,

poyembekeza thandizo chabe;

kudikira tinadikira mtundu wosatha kupulumutsa.

18 Amalondola mapazi athu, sitingayende m’makwalala athu;

chitsiriziro chathu chayandikira, masiku athu akwaniridwa;

pakuti chitsiriziro chathu chafikadi.

19 Otilondola anaposa ziombankhanga

za m’mlengalenga m’liwiro lao,

anatithamangitsa pamapiri natilalira m’chipululu.

20 Wodzozedwa wa Yehova,

ndiye mpweya wa m’mphuno mwathu,

anagwidwa m’maenje ao;

amene tinanena kuti,

Tidzakhala m’mthunzi mwake pakati pa amitundu,

21 kondwera nusangalale, mwana wamkazi wa Edomu,

wokhala m’dziko la Uzi;

chikho chidzapita ngakhale mwa iwenso;

udzaledzera ndi kuvula zako.

22 Mphulupulu yako yatha, mwana wamkazi wa Ziyoni,

Yehova sadzakutenganso ndende;

koma adzazonda mphulupulu yako, mwana wa mkazi wa Edomu,

nadzavumbulutsa zochimwa zako.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/LAM/4-9251eb354beca9579bd87a69a3e2e0d9.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *