Oipa adzalangidwa, okoma adzadalitsidwa. Asamale chilamulo; adzafika Eliya
1 Pakuti taonani, likudza tsiku, lotentha ngati ng’anjo; ndipo onse akudzikuza ndi onse akuchita choipa. Adzakhala ngati chiputu; ndi tsiku lilinkudza lidzawayatsa, ati Yehova wa makamu, osawasiyira muzu kapena nthambi.
2 Koma inu akuopa dzina langa, dzuwa la chilungamo lidzakutulukirani, muli kuchiritsa m’mapiko mwake; ndipo mudzatuluka ndi kutumphatumpha ngati anaang’ombe onenepa otuluka m’khola.
3 Ndipo mudzapondereza oipa; pakuti adzakhala ngati mapulusa kumapazi anu, tsiku ndidzaikalo, ati Yehova wa makamu.
4 Kumbukirani chilamulo cha Mose mtumiki wanga, ndinamlamuliracho mu Horebu chikhale cha Israele yense, ndicho malemba ndi maweruzo.
5 Taonani, ndidzakutumizirani Eliyamnenerilisanadze tsiku lalikulu ndi loopsa la Yehova.
6 Ndipo adzabwezera mitima ya atate kwa ana, ndi mitima ya ana kwa atate ao; kuti ndisafike ndi kukantha dziko lionongeke konse.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MAL/4-2b57f622ee755e75b295c6e1107275a1.mp3?version_id=1068—