Categories
MACHITIDWE

MACHITIDWE 9

Kusandulika mtima kwa Saulo panjira ya ku Damasiko

1 Koma Saulo, wosaleka kupumira paophunziraa Ambuye kuopsa ndi kupha, ananka kwa mkulu wa ansembe,

2 napempha kwa iye makalata akunka nao ku Damasiko ku masunagoge, kuti akapeza ena otsata Njirayo, amuna ndi akazi, akawatenge kudza nao omangidwa kuYerusalemu.

3 Ndipo poyenda ulendo wake, kunali kuti iye anayandikira Damasiko: ndipo mwadzidzidzi kudawala momzingira kuunika kochokera kumwamba;

4 ndipo anagwa pansi, namva mau akunena naye, Saulo, Saulo, Undilondalonderanji?

5 Koma anati, Ndinu yani Mbuye? Ndipo anati, Ndine Yesu amene umlondalonda;

6 komatu, uka, nulowe m’mzinda, ndipo kudzanenedwa kwa iwe chimene uyenera kuchita.

7 Ndipo amunawo akumperekeza iye anaima duu, atamvadi mau, koma osaona munthu.

8 Ndipo Saulo anauka; koma potseguka maso ake, sanapenye kanthu; ndipo anamgwira dzanja, namtenga nalowa naye mu Damasiko.

9 Ndipo anakhala masiku atatu wosaona, ndipo sanadye kapena kumwa.

10 Koma ku Damasiko kunali wophunzira wina dzina lake Ananiya; ndipo Ambuye anati kwa iye m’masomphenya, Ananiya. Ndipo anati, Ndili pano, Ambuye,

11 Ndipo Ambuye anati kwa iye, Tauka, pita ku khwalala lotchedwa Lolunjika, ndipo m’nyumba ya Yudasi ufunse za munthu dzina lake Saulo, wa ku Tariso: pakuti taona, alikupemphera

12 ndipo anaona mwamuna dzina lake Ananiya, alikulowa, namuika manja, kuti apenyenso.

13 Ndipo Ananiya anayankha nati, Ambuye, ndamva ndi ambiri za munthu uyu, kuti anachitiradi choipa oyera mtima anu mu Yerusalemu;

14 ndi kuti pano ali nao ulamuliro wa kwa ansembe aakulu wakumanga onse akuitana pa dzina lanu.

15 Koma Ambuye anati kwa iye, Pita; pakuti iye ndiye chotengera changa chosankhika, chakunyamula dzina langa pamaso paamitundundi mafumu ndi ana a Israele;

16 pakuti Ine ndidzamuonetsa iye zinthu zambiri ayenera iye kuzimva kuwawa chifukwa cha dzina langa.

17 Ndipo anachoka Ananiya, nalowa m’nyumbayo; ndipo anaika manja ake pa iye, nati, Saulo, mbale, Ambuye wandituma ine, ndiye Yesu amene anakuonekerani panjira wadzerayo, kuti upenyenso, ndi kudzazidwa ndi Mzimu Woyera.

18 Ndipo pomwepo padagwa kuchoka m’maso mwake ngati mamba, ndipo anapenyanso; ndipo ananyamuka nabatizidwa;

19 ndipo analandira chakudya, naona nacho mphamvu.

Azunzika mzunziyo

Ndipo anakhala pamodzi ndi ophunzira a ku Damasiko masiku ena.

20 Ndipo pomwepo m’masunagoge analalikira Yesu, kuti Iye ndiye Mwana wa Mulungu.

21 Ndipo onse amene anamva anadabwa, nanena, Suyu iye amene anaononga mu Yerusalemu onse akuitana pa dzina ili? Ndipo wadza kuno kudzatero, kuti amuke nao omangidwa kwa ansembe aakulu.

22 Koma Saulo anakula makamaka mumphamvu, nadodometsa Ayuda akukhala mu Damasiko, nawatsimikizira kuti ameneyo ndiKhristu.

23 Ndipo atapita masiku ambiri, Ayuda anapangana kuti amuphe iye;

24 koma chiwembu chao chinadziwika ndi Saulo. Ndipo anadikiranso pazipata usana ndi usiku kuti amuphe;

25 koma ophunzira ake anamtenga usiku, nampyoletsa palinga, namtsitsa mu dengu.

26 Koma m’mene anafika ku Yerusalemu, anayesa kudziphatika kwa ophunzira; ndipo anamuopa iye onse, osakhulupirira kuti ali wophunzira.

27 Koma Barnabasi anamtenga, napita naye kwaatumwi, nawafotokozera umo adaonera Ambuye m’njira, ndi kuti analankhula naye, ndi kuti mu Damasiko adanena molimbika mtima m’dzina la Yesu.

28 Ndipo anali pamodzi nao, nalowa natuluka ku Yerusalemu, nanena molimbika mtima m’dzina la Ambuye;

29 ndipotu analankhula natsutsana ndi Agriki; koma anayesayesa kumupha iye.

30 Koma m’mene abale anachidziwa, anapita naye ku Kesareya, namtumiza achokeko kunka ku Tariso.

31 Pamenepo ndipoMpingowa mu Yudeya yense ndi Galileya ndi Samariya unali nao mtendere, nukhazikika; ndipo unayenda m’kuopa kwa Ambuye ndi m’chitonthozo cha Mzimu Woyera, nuchuluka.

Achiritsidwa Eneya; aukitsidwa Tabita

32 Koma kunali, pakupita Petro ponseponse, anatsikiranso kwa oyera mtima akukhala ku Lida.

33 Ndipo anapeza kumeneko munthu dzina lake Eneya, amene anagonera pamphasa zaka zisanu ndi zitatu; amene anagwidwa manjenje.

34 Ndipo Petro anati kwa iye, Eneya, Yesu Khristu akuchiritsa iwe; uka, yalula mphasa yako. Ndipo anauka pomwepo.

35 Ndipo anamuona iye onse akukhala ku Lida ndi ku Saroni, natembenukira kwa Ambuye amenewa.

36 Koma mu Yopa munali wophunzira dzina lake Tabita, ndilo kunena Dorika; mkazi ameneyo anadzala ndi ntchito zabwino ndi zachifundo zimene anazichita.

37 Ndipo kunali m’masiku awa, kuti anadwala iye, namwalira; ndipo atamsambitsa iye anamgoneka m’chipinda chapamwamba.

38 Ndipo popeza Lida ndi pafupi pa Yopa, m’mene anamva ophunzirawo kuti Petro anali pomwepo, anamtumizira anthu awiri, namdandaulira, Musachedwa mudze kwa ife.

39 Ndipo Petro ananyamuka, napita nao. M’mene anafikako, anapita naye kuchipinda chapamwamba; ndipo amasiye onse anaimirirapo pali iye, nalira, namuonetsa malaya ndi zovala zimene Dorika adasoka, pamene anali nao pamodzi.

40 Koma Petro anawatulutsa onse, nagwada pansi, napemphera; ndipo potembenukira kumtembo anati, Tabita, uka. Ndipo anatsegula maso ake; ndipo pakuona Petro, anakhala tsonga.

41 Ndipo Petro anamgwira dzanja, namnyamutsa; ndipo m’mene adaitana oyera mtima ndi amasiye, anampereka iye wamoyo.

42 Ndipo kudadziwika ku Yopa konse: ndipo ambiri anakhulupirira Ambuye.

43 Ndipo kunali, kuti anakhala iye mu Yopa masiku ambiri ndi munthu Simoni wofufuta zikopa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ACT/9-2039bced8cb78d90f6f7ac6664f28c82.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *