Uthenga Wabwino pa Samariya. Simoni wanyanga
1 Ndipo Saulo analikuvomerezana nao pa imfa yake. Ndipo tsikulo kunayamba kuzunza kwakukulu paMpingounali muYerusalemu; ndipo anabalalitsidwa onse m’maiko a Yudeya ndi Samariya, koma osatiatumwiai.
2 Ndipo anamuika Stefano anthu opembedza, namlira maliro aakulu.
3 Ndipo Saulo anapasula Mpingo, nalowa nyumba ndi nyumba, nakokamo amuna ndi akazi, nawaika m’ndende.
4 Pamenepo ndipo iwo akubalalitsidwa anapitapita nalalikira mauwo.
5 Ndipo Filipo anatsikira kumzinda wa ku Samariya, nawalalikira iwoKhristu.
6 Ndipo makamuwo ndi mtima umodzi anasamalira zonenedwa ndi Filipo, pamene anamva, napenya zizindikiro zimene anazichita.
7 Pakuti ambiri a iwo akukhala nayo mizimu yonyansa inawatulukira, yofuula ndi mau aakulu; ndipo ambiri amanjenje, ndi opunduka, anachiritsidwa.
8 Ndipo panakhala chimwemwe chachikulu m’mzindamo.
9 Koma panali munthu dzina lake Simoni amene adachita matsenga m’mzindamo kale, nadabwitsa anthu a Samariya, ndi kunena kuti iye yekha ndiye munthu wamkulu;
10 ameneyo anamsamalira onsewo, kuyambira wamng’ono kufikira wamkulu, ndi kunena, Uyu ndiye mphamvu ya Mulungu, yonenedwa Yaikulu.
11 Ndipo anamsamalira iye, popeza nthawi yaikulu adawadabwitsa iwo ndi matsenga ake.
12 Koma pamene anakhulupirira Filipo wakulalikira Uthenga Wabwino wa Ufumu wa Mulungu ndi dzina la Yesu Khristu, anabatizidwa, amuna ndi akazi.
13 Ndipo Simoni mwini wake anakhulupiriranso: ndipo m’mene anabatizidwa, anakhalira ndi Filipo; ndipo pakuona zizindikiro ndi mphamvu zazikulu zilikuchitika, anadabwa.
14 Koma pamene atumwi a ku Yerusalemu anamva kuti Samariya adalandira mau a Mulungu, anawatumizira Petro ndi Yohane;
15 amenewo, m’mene adatsikirako, anawapempherera, kuti alandire Mzimu Woyera:
16 pakuti kufikira pamenepo nkuti asanagwe pa wina mmodzi wa iwo; koma anangobatizidwa m’dzina la Ambuye Yesu.
17 Pamenepo anaika manja pa iwo, ndipo analandira Mzimu Woyera.
18 Koma pakuona Simoni kuti mwa kuika manja a atumwi anapatsidwa Mzimu Woyera, anawatengera ndalama,
19 nanena, Ndipatseni inenso ulamuliro umene, kuti aliyense amene ndikaika manja pa iye, alandire Mzimu Woyera.
20 Koma Petro anati kwa iye, Ndalama yako itayike nawe, chifukwa unalingirira kulandira mphatso ya Mulungu ndi ndalama.
21 Ulibe gawo kapena cholandira ndi mau awa; pakuti mtima wako suli wolunjika pamaso pa Mulungu.
22 Chifukwa chake lapa choipa chako ichi, pemphera Ambuye, kuti kapena akukhululukire iwe cholingirira cha mtima wako.
23 Pakuti ndiona kuti wagwidwa ndi ndulu yowawa ndi nsinga ya chosalungama.
24 Ndipo Simoni anayankha nati, Mundipempherere ine kwa Ambuye kuti zisandigwere izi mwanenazi.
25 Pamenepo iwo, atatha kuchita umboni ndi kulankhula mau a Ambuye, anabwera kunka ku Yerusalemu, nalalikira Uthenga Wabwino kumidzi yambiri yaAsamariya.
Filipo ndi mdindo wa ku Etiopiya
26 Komamngelowa Ambuye analankhula ndi Filipo, nanena, Nyamuka, nupite mbali ya kumwera, kutsata njira yotsika kuchokera ku Yerusalemu kunka ku Gaza; ndiyo ya chipululu.
27 Ndipo ananyamuka napita; ndipo taona munthu wa ku Etiopiya, mdindo wamphamvu wa Kandake, mfumu yaikazi ya Aetiopiya, ndiye wakusunga chuma chake chonse, amene anadza ku Yerusalemu kudzapemphera;
28 ndipo analinkubwerera, nalikukhala pa galeta wake, nawerengamneneriYesaya.
29 Ndipo Mzimu anati kwa Filipo, Yandikira, nudziphatike kugaleta uyu.
30 Ndipo Filipo anamthamangira, namva iye alikuwerenga Yesaya mneneri, ndipo anati, Kodi muzindikira chimene muwerenga?
31 Koma anati, Ndingathe bwanji, popanda munthu wonditsogolera ine? Ndipo anapempha Filipo akwere nakhale naye.
32 Koma palembo pamene analikuwerengapo ndipo:
Ngati nkhosa anatengedwa kukaphedwa,
ndi mongamwanawankhosaali duu pamaso pa womsenga,
kotero sanatsegule pakamwa pake.
33 M’kuchepetsedwa kwake chiweruzo chake chinachotsedwa;
mbadwo wake adzaubukitsa ndani?
Chifukwa wachotsedwa kudziko moyo wake.
34 Ndipo mdindoyo anayankha Filipo, nati, Ndikupempha, mneneri anena ichi za yani? Za yekha, kapena za wina?
35 Ndipo Filipo anatsegula pakamwa pake, nayamba pa lembo ili, nalalikira kwa iye Yesu.
36 Ndipo monga anapita panjira pao, anadza kumadzi akuti; ndipo mdindoyo anati, Taonapo madzi; chindiletsa ine chiyani ndisabatizidwe?
38 Ndipo anamuuza kuti aimitse galeta; ndipo anatsikira onse awiri kumadzi, Filipo ndi mdindoyo; ndipo anambatiza iye.
39 Ndipo pamene anakwera kutuluka m’madzi, Mzimu wa Ambuye anakwatula Filipo; ndipo mdindo sanamuonenso, pakuti anapita njira yake wokondwera.
40 Koma Filipo anapezedwa ku Azoto; ndipo popitapita analalikira Uthenga Wabwino m’midzi yonse, kufikira anadza iye ku Kesareya.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ACT/8-fd3842d197227cd51ea532457f22b8e3.mp3?version_id=1068—