Asankha atumiki asanu ndi awiri
1 Koma masiku awo, pakuchulukitsaophunzira, kunauka chidandaulo, Agriki kudandaula pa Ahebri, popeza amasiye ao anaiwalika pa chitumikiro cha tsiku ndi tsiku.
2 Ndipo khumi ndi awiriwo anaitana unyinji wa ophunzira, nati, Sikuyenera kuti ife tisiye kulalikira mau a Mulungu ndi kutumikira podyerapo.
3 Chifukwa chake, abale, yang’anani mwa inu amuna asanu ndi awiri a mbiri yabwino, odzala ndi Mzimu ndi nzeru, amene tikawaike asunge ntchito iyi.
4 Koma ife tidzalimbika m’kupemphera, ndi kutumikira mau.
5 Ndipo mau amene anakonda unyinji wonse; ndipo anasankha Stefano, ndiye munthu wodzala ndi chikhulupiriro ndi Mzimu Woyera, ndi Filipo, ndi Prokoro, ndi Nikanore ndi Timoni, ndi Parmenasi, ndi Nikolasi, ndiye wopinduka wa ku Antiokeya:
6 amenewo anawaika pamaso paatumwi; ndipo m’mene adapemphera, anaika manja pa iwo.
7 Ndipo mau a Mulungu anakula; ndipo chiwerengero cha ophunzira chidachulukatu kuYerusalemu; ndipo khamu lalikulu la ansembe linamvera chikhulupirirocho.
Stefano woyamba wophedwa chifukwa cha Khristu
8 Ndipo Stefano, wodzala ndi chisomo ndi mphamvu, anachita zozizwa ndi zizindikiro zazikulu mwa anthu.
9 Koma anauka ena a iwo ochokera m’sunagogewa Alibertino, ndi Akirene, ndi Aaleksandriya, ndi mwa iwo a ku Silisiya ndi ku Asiya, natsutsana ndi Stefano.
10 Ndipo sanathe kuipambana nzeru ndi Mzimu amene analankhula naye.
11 Pamenepo anafuna anthu akumpitira pansi, ndi kuti, Tidamumva iye alikunenera Mose ndi Mulungu mau amwano.
12 Ndipo anautsa anthu, ndi akulu, ndi alembi, namfikira, namgwira iye, nadza naye kubwalo la akulu a milandu,
13 naimika mboni zonama, zakunena, Munthu ameneyo saleka kunenera malo oyera amene, ndi chilamulo;
14 pakuti tinamumva iye alikunena, kuti, Yesu Mnazarayo amene adzaononga malo ano, nadzasanduliza miyambo imene Mose anatipatsa.
15 Ndipo anampenyetsetsa onse akukhala m’bwalo la akulu a milandu, naona nkhope yake ngati nkhope yamngelo.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ACT/6-e007e06b172b12613c28467f8679e022.mp3?version_id=1068—