Categories
MACHITIDWE

MACHITIDWE 4

Petro ndi Yohane ku bwalo la akulu

1 Koma m’mene analikulankhula ndi anthu, ansembe ndi mdindo wa ku Kachisi ndiAsadukianadzako,

2 ovutika mtima chifukwa anaphunzitsa anthuwo, nalalikira mwa Yesu kuuka kwa akufa.

3 Ndipo anawathira manja, nawaika m’ndende kufikira m’mawa; pakuti mpa madzulo pamenepo.

4 Koma ambiri a iwo amene adamva mau anakhulupirira; ndipo chiwerengero cha amuna chinali ngati zikwi zisanu.

5 Koma panali m’mawa mwake, anasonkhana pamodzi muYerusalemuoweruza, ndi akulu, ndi alembi;

6 ndi Anasi mkulu wa ansembe, ndi Kayafa, ndi Yohane, ndi Aleksandro, ndi onse amene anali a fuko la mkulu wa ansembe.

7 Ndipo m’mene anawaimika pakati, anafunsa kuti, Ndi mphamvu yanji, kapena m’dzina lanji, mwachita ichi inu?

8 Pamenepo Petro, wodzala ndi Mzimu Woyera anati kwa iwo, Oweruza a anthu inu, ndi akulu,

9 ngati ife lero tiweruzidwa chifukwa cha ntchito yabwino ya pa munthu wodwala, ndi machiritsidwe ake,

10 zindikirani inu nonse, ndi anthu onse a Israele, kuti m’dzina la YesuKhristuMnazarayo, amene inu munampachika pamtanda, amene Mulungu anamuukitsa kwa akufa, mwa Iyeyu munthuyu aimirirapo pamaso panu, wamoyo.

11 Iye ndiye mwalawo woyesedwa wopanda pake ndi inu omanga nyumba, umene unayesedwa mutu wa pangodya.

12 Ndipo palibe chipulumutso mwa wina yense, pakuti palibe dzina lina pansi pa thambo la kumwamba, lopatsidwa mwa anthu, limene tiyenera kupulumutsidwa nalo.

13 Koma pakuona kulimbika mtima kwa Petro ndi Yohane, ndipo pozindikira kuti ndiwo anthu osaphunzira ndi opulukira, anazizwa ndipo anawazindikira, kuti adakhala pamodzi ndi Yesu.

14 Ndipotu pakuona munthu wochiritsidwayo alikuimirira pamodzi nao, analibe kanthu kakunena kotsutsa.

15 Koma pamene anawalamulira iwo achoke m’bwalo la akulu a milandu, ananena wina ndi mnzake,

16 kuti, Tidzawachitira chiyani anthu awa? Pakutitu chaoneka kwa onse akukhala mu Yerusalemu kuti chizindikiro chozindikirika chachitidwa ndi iwo, ndipo sitingathe kukana.

17 Komatu tiwaopse asalankhulenso m’dzina ili kwa munthu aliyense, kuti chisabukenso kwa anthu.

18 Ndipo anawaitana, nawalamulira kuti asanene konse kapena kuphunzitsa m’dzina la Yesu.

19 Koma Petro ndi Yohane anayankha nati kwa iwo, Weruzani, ngati nkwabwino pamaso pa Mulungu kumvera inu koposa Mulungu;

20 pakuti sitingathe ife kuleka kulankhula zimene tinaziona ndi kuzimva.

21 Koma m’mene anawaopsanso anawamasula, osapeza kanthu kakuwalanga, chifukwa cha anthu; pakuti onse analemekeza Mulungu chifukwa cha chomwe chidachitika.

22 Pakuti anali wa zaka zake zoposa makumi anai munthuyo, amene chizindikiro ichi chakumchiritsa chidachitidwa kwa iye.

Okhulupirira athamangira kupemphera

23 Ndipo m’mene anamasulidwa, anadza kwa anzao a iwo okha, nawauza zilizonse ansembe aakulu ndi akulu adanena nao.

24 Ndipo m’mene adamva, anakweza mau kwa Mulungu ndi mtima umodzi, nati, Mfumu, Inu ndinu wolenga thambo la kumwamba ndi dziko, ndi nyanja, ndi zonse zili m’menemo;

25 amene mwa Mzimu Woyera, pakamwa pa kholo lathu Davide mtumiki wanu, mudati,

Amitunduanasokosera chifukwa chiyani?

Nalingirira zopanda pake anthu?

26 Anadzindandalitsa mafumu a dziko,

ndipo oweruza anasonkhanidwa pamodzi,

kutsutsana ndi Ambuye, ndi Khristu wake.

27 Pakuti zoonadi anasonkhanidwa m’mzinda munoHerode, ndi Pontio Pilato yemwe pamodzi ndi amitundu ndi anthu a Israele kumchitira choipa Mwana wanu wopatulika Yesu amene munamdzoza;

28 kuti achite zilizonse dzanja lanu ndi uphungu wanu zidaweruziratu zichitike.

29 Ndipo tsopano Ambuye, penyani mau ao akuopsa, ndipo patsani kwa akapolo anu alankhule mau anu ndi kulimbika mtima konse,

30 m’mene mutambasula dzanja lanu kukachiritsa; ndi kuti zizindikiro ndi zozizwa zichitidwe mwa dzina la Mwana wanu wopatulika Yesu.

31 Ndipo m’mene adapemphera iwo, panagwedezeka pamalo pamene adasonkhanirapo; ndipo anadzazidwa onse ndi Mzimu Woyera, nalankhula mau a Mulungu molimbika mtima.

Madyerano a Akhristu oyamba

32 Ndipo unyinji wa iwo akukhulupirira anali wa mtima umodzi ndi moyo umodzi; ndipo sananene mmodzi kuti kanthu ka chuma anali nacho ndi kake ka iye yekha; koma anali nazo zonse zodyerana.

33 Ndipoatumwianachita umboni ndi mphamvu yaikulu za kuuka kwa Ambuye Yesu; ndipo panali chisomo chachikulu pa iwo onse.

34 Pakuti mwa iwo munalibe wosowa; pakuti onse amene anali nayo minda, kapena nyumba, anazigulitsa nabwera nao malonda ake a izo adazigulitsa,

35 nawaika pa mapazi a atumwi; ndipo anagawira yense monga kusowa kwake.

36 Ndipo Yosefe, wotchedwa ndi atumwi Barnabasi (ndilo losandulika mwana wa chisangalalo), Mlevi, fuko lake la ku Kipro,

37 pokhala nao munda, anaugulitsa, nabwera nazo ndalama zake, naziika pa mapazi a atumwi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ACT/4-ed5119da8347e112edb9418b5abc49ff.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *