Categories
MACHITIDWE

MACHITIDWE 3

Wopunduka chibadwire achiritsidwa. Chonenera Petro mu Kachisi

1 Koma Petro ndi Yohane analikukwera kunka ku Kachisi pa ora lakupembedza, ndilo lachisanu ndi chinai.

2 Ndipo munthu wina wopunduka miyendo chibadwire ananyamulidwa, amene akamuika masiku onse pa khomo la Kachisi lotchedwa Lokongola, kuti apemphe zaulere kwa iwo akulowa mu Kachisi;

3 ameneyo, pakuona Petro ndi Yohane akuti alowe mu Kachisi, anapempha alandire chaulere.

4 Ndipo Petro, pompenyetsetsa iye pamodzi ndi Yohane, anati, Tiyang’ane ife.

5 Ndipo iye anavomereza iwo, nalingirira kuti adzalandira kanthu.

6 Koma Petro anati,Silivandi golide ndilibe; koma chimene ndili nacho, ichi ndikupatsa, M’dzina la YesuKhristuMnazarayo, yenda.

7 Ndipo anamgwira iye kudzanja lake lamanja, namnyamutsa; ndipo pomwepo mapazi ake ndi mfundo za kumapazi zinalimbikitsidwa.

8 Ndipo anazunzuka, naimirira, nayenda; ndipo analowa pamodzi nao mu Kachisi, nayenda, nalumpha, nayamika Mulungu.

9 Ndipo anthu onse anamuona iye, alikuyenda ndi kuyamika Mulungu;

10 namzindikira iye, kuti ndiye amene anakhala pa Chipata Chokongola cha Kachisi: ndipo anadzazidwa ndi kudabwa ndi kuzizwa pa ichi chidamgwera.

11 Koma m’mene anagwira Petro ndi Yohane, anawathamangira pamodzi anthu onse kukhonde lotchedwa la Solomoni, alikudabwa ndithu.

12 Koma m’mene Petro anachiona, anayankha kwa anthu, Amuna inu a Israele, muzizwa naye bwanji ameneyo? Kapena mutipenyetsetsa ife bwanji, monga ngati tamyendetsa iye ndi mphamvu ya ife eni, kapena ndi chipembedzo chathu?

13 Mulungu wa Abrahamu, ndi Isaki, ndi Yakobo, Mulungu wa makolo athu, analemekeza Mwana wake Yesu; amene inu munampereka ndi kumkaniza pa Pilato, poweruza iyeyu kummasula.

14 Koma inu munakaniza Woyera ndi Wolungamayo, ndipo munapempha kuti munthu wambanda apatsidwe kwa inu,

15 ndipo munamupha Mkulu wa moyo; amene Mulungu anamuukitsa kwa akufa; za ichi ife tili mboni.

16 Ndipo pa chikhulupiriro cha m’dzina lake dzina lakelo linalimbikitsa iye amene mumuona, nimumdziwa; ndipo chikhulupiriro chili mwa Iye chinampatsa kuchira konse kumeneku pamaso pa inu nonse.

17 Ndipo tsopano, abale, ndidziwa kuti munachichita mosadziwa, monganso akulu anu.

18 Koma zimene Mulungu analalikiratu m’kamwa mwa aneneri onse, kuti adzamva kuwawa Khristu, Iye anakwaniritsa chotero.

19 Chifukwa chake lapani, bwererani kuti afafanizidwe machimo anu, kotero kuti zidze nyengo zakutsitsimutsa zochokera kunkhope ya Ambuye;

20 ndipo atume amene anaikidwa kwa inu, Khristu Yesu;

21 amene thambo la kumwamba liyenera kumlandira kufikira nthawi zakukonzanso zinthu zonse, zimene Mulungu analankhula za izo m’kamwa mwa aneneri ake oyera chiyambire.

22 Mosetu anati, Mbuye Mulungu adzaukitsira inumnenerimwa abale anu, ngati ine; mudzamvera iye m’zinthu zilizonse akalankhule nanu.

23 Ndipo kudzali, kuti wamoyo aliyense samvera mneneri ameneyu, adzasakazidwa konse mwa anthu.

24 Koma angakhale aneneri onse kuyambira Samuele ndi akumtsatira, onse amene analankhula analalikira za masiku awa.

25 Inu ndinu ana a aneneri, ndi a panganolo Mulungu anapangana ndi makolo anu ndi kunena kwa Abrahamu, Ndipo mu mbeu yako mafuko onse a dziko adzadalitsidwa.

26 Kuyambira ndi inu, Mulungu, ataukitsa Mwana wake, anamtuma kukudalitsani inu, ndi kukubwezani yense ku zoipa zake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ACT/3-88753cdfda64a6c347786148f32cce71.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *