1 NdipoAgripaanati kwa Paulo, Kwaloleka udzinenere wekha. Pamenepo Paulo, anatambasula dzanja nadzikanira:
2 Ndidziyesera wamwai, Mfumu Agripa, popeza nditi ndidzikanira lero pamaso panu, za zonse zimene Ayuda andinenera nazo;
3 makamaka popeza mudziwitsa miyambo yonse ndi mafunso onse a mwa Ayuda; chifukwa chake ndikupemphani mundimvere ine moleza mtima.
4 Mayendedwe a moyo wanga tsono, kuyambira pa chibwana changa, amene anakhala chiyambire mwa mtundu wanga muYerusalemu, awadziwa Ayuda onse;
5 andidziwa ine chiyambire, ngati afuna kuchitapo umboni, kuti ndinakhalaMfarisimonga mwa mpatuko wolunjikitsitsa wa chipembedzero chathu.
6 Ndipo tsopano ndiimirira pano ndiweruzidwe pa chiyembekezo cha lonjezano limene Mulungu analichita kwa makolo athu;
7 kufikira komweko mafuko athu khumi ndi awiri, potumikira Mulungu kosapumula usiku ndi usana, ayembekeza kufikirako. Chifukwa cha chiyembekezo ichi, Mfumu, andinenera Ayuda.
8 Muchiyesa chinthu chosakhulupirika, chakuti Mulungu aukitsa akufa?
9 Inedi ndinayesa ndekha, kuti kundiyenera kuchita zinthu zambiri zotsutsana nalo dzina la Yesu Mnazarayo.
10 Chimenenso ndinachita mu Yerusalemu: ndipo ndinatsekera ine oyera mtima ambiri m’ndende, popeza ndidalandira ulamuliro wa kwa ansembe aakulu; ndiponso pophedwa iwo, ndinavomerezapo.
11 Ndipo ndinawalanga kawirikawiri m’masunagogeonse, ndi kuwakakamiza anene zamwano; ndipo pakupsa mtima kwakukulu pa iwo ndinawalondalonda ndi kuwatsata ngakhale kufikira kumizinda yakunja.
12 M’menemo popita ine ku Damasiko ndi ulamuliro ndi ukumu wa kwa ansembe aakulu,
13 dzuwa lamsana, ndinaona panjira, Mfumu, kuunika kochokera kumwamba kowalitsa koposa dzuwa kunawala pondizinga ine ndi iwo akundiperekeza.
14 Ndipo pamene tidagwa pansi tonse, ndinamva mau akunena kwa ine m’chinenedwe cha Chihebri, Saulo, Saulo, undilondalonderanji Ine? Nkukuvuta kutsalima pachotwikira.
15 Ndipo ndinati, Ndinu yani Mbuye? Ndipo Ambuye anati, Ine ndine Yesu amene iwe umlondalonda.
16 Komatu uka, imirira pa mapazi ako; pakuti chifukwa cha ichi ndinaonekera kwa iwe, kukuika iwe ukhale mtumiki ndi mboni ya izi wandionamo Ine, ndiponso ya izi ndidzakuonekeramo iwe;
17 ndi kukulanditsa kwa anthu, ndi kwaamitundu, amene Ine ndikutuma kwa iwo,
18 kukawatsegulira maso ao, kuti atembenuke kuchokera kumdima, kulinga kukuunika, ndi kuchokera ulamuliro waSatanakulinga kwa Mulungu, kuti alandire iwo chikhululukiro cha machimo, ndi cholowa mwa iwo akuyeretsedwa ndi chikhulupiriro cha mwa Ine.
19 Potero, Mfumu Agripa, sindinakhale ine wosamvera masomphenya a Kumwamba;
20 komatu kuyambira kwa iwo a mu Damasiko, ndi a mu Yerusalemu, ndi m’dziko lonse la Yudeya, ndi kwa amitundunso ndinalalikira kuti alape, natembenukire kwa Mulungu, ndi kuchita ntchito zoyenera kutembenuka mtima.
21 Chifukwa cha izi Ayuda anandigwira mu Kachisi, nayesa kundipha.
22 Pamenepo pothandizidwa ndi Mulungu, ndiimirira kufikira lero lino, ndi kuwachitira umboni ang’ono ndi akulu, osanena kanthu kena koma zimene aneneri ndi Mose ananena zidzafika;
23 kutiKhristuakamve zowawa, kuti Iye, woyamba mwa kuuka kwa akufa, adzalalikira kuunika kwa anthu ndi kwa amitundu.
24 Koma pakudzikanira momwemo, Fesito anati ndi mau aakulu, Uli wamisala Paulo; kuwerengetsa kwako kwakuchititsa misala.
25 Koma Paulo anati, Ndilibe misala, Fesito womvekatu; koma nditulutsa mau a choonadi ndi odziletsa.
26 Pakuti mfumuyo idziwa izi, kwa iye imene ndilankhula nayonso mosaopa: pakuti ndidziwadi kuti kulibe kanthu ka izi kadambisikira; pakuti ichi sichinachitike m’tseri.
27 Mfumu Agripa, mukhulupirira aneneri kodi? Ndidziwa kuti muwakhulupirira.
28 Ndipo Agripa anati kwa Paulo, Ndi kundikopa pang’ono ufuna kundiyesera Mkhristu.
29 Ndipo Paulo anati, Mwenzi atalola Mulungu, kuti ndi kukopa pang’ono, kapena ndi kukopa kwambiri, si inu nokha, komatunso onse akundimva ine lero, akadakhala otero onga ndili ine, osanena nsinga izi.
30 Ndipo ananyamuka mfumu, ndi kazembe, ndi Berenise, ndi iwo akukhala nao;
31 ndipo atapita padera analankhula wina ndi mnzake, nanena, Munthu uyu sanachite kanthu koyenera imfa, kapena nsinga.
32 Ndipo Agripa anati kwa Fesito, Tikadakhoza kumasula munthuyu, akadapanda kunena, Ndikatulukire kwaKaisara.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ACT/26-70b689c39d51cfea0d689c3eb85aba48.mp3?version_id=1068—