Categories
MACHITIDWE

MACHITIDWE 19

Ulendo wachitatu wa Paulo. Demetrio autsa phokoso

1 Ndipo panali, pamene Apolo anali ku Korinto, Paulo anapita pa maiko a pamtunda, nafika ku Efeso, napezaophunziraena;

2 ndipo anati kwa iwo, Kodi munalandira Mzimu Woyera pamene munakhulupirira? Ndipo anati, Iai, sitinamve konse kuti Mzimu Woyera waperekedwa.

3 Ndipo anati, Nanga mwabatizidwa m’chiyani? Ndipo anati, Mu ubatizo wa Yohane.

4 Ndipo anati Paulo, Yohane anabatiza ndi ubatizo wa kutembenuka mtima, nati kwa anthu, kuti amkhulupirire Iye amene adzadza pambuyo pake, ndiye Yesu.

5 Pamene anamva ichi, anabatizidwa m’dzina la Ambuye Yesu.

6 Ndipo pamene Paulo anaika manja ake pa iwo, Mzimu Woyera anadza pa iwo; ndipo analankhula ndi malilime, nanenera.

7 Onsewo anali ngati amuna khumi ndi awiri.

8 Ndipo iye analowa m’sunagoge, nanena molimba mtima, miyezi itatu, natsutsana ndi kukopa kunena za Ufumu wa Mulungu.

9 Koma pamene ena anaumitsa mtima ndi kusamvera, nanenera zoipa Njirayo pamaso pa anthu, anawachokera, napatutsa ophunzira, nafotokozera masiku onse m’sukulu ya Tirano.

10 Ndipo anachita chomwecho zaka ziwiri; kotero kuti onse akukhala mu Asiya anamva mau a Ambuye, Ayuda ndi Agriki.

11 Ndipo Mulungu anachita zamphamvu za pazokha ndi manja a Paulo;

12 kotero kuti anamuka nazo kwa odwala nsalu zopukutira ndi za pantchito, zochokera pathupi pake, ndipo nthenda zinawachokera, ndi ziwanda zinatuluka.

13 Koma Ayuda enanso oyendayenda, otulutsa ziwanda, anadziyesa kutchula pa iwo amene anali ndi ziwanda dzina la Ambuye Yesu, kuti, Ndikulumbirirani pa Yesu amene amlalika Paulo.

14 Ndipo panali ana aamuna asanu ndi awiri a Skeva, Myuda, mkulu wa ansembe amene anachita ichi.

15 Ndipo unayankha mzimu woipa, nuti kwa iwo, Yesu ndimzindikira, ndi Paulo ndimdziwa, koma inu ndinu ayani?

16 Ndipo munthu, mwa iye amene munali mzimu woipa, anawalumphira nawaposa, nawagonjetsa onsewo, kotero kuti anathawa m’nyumba amaliseche ndi olasidwa.

17 Zimenezo zidamveka kwa onse, Ayuda ndi Agriki, amene anakhala ku Efeso; ndipo mantha anagwera onsewo, ndipo dzina la Ambuye Yesu linakuzika.

18 Ndipo ambiri a iwo akukhulupirirawo anadza, navomereza, nafotokoza machitidwe ao.

19 Ndipo ambiri a iwo akuchita zamatsenga anasonkhanitsa mabuku ao, nawatentha pamaso pa onse; ndipo anawerenga mtengo wake, napeza ndalama zasilivazikwi makumi asanu.

20 Chotero mau a Ambuye anachuluka mwamphamvu napambana.

21 Ndipo zitatha izi, Paulo anatsimikiza mu mzimu wake, atapita pa Masedoniya ndiAkaya, kunka kuYerusalemu, kuti, Nditamuka komweko ndiyenera kuonanso ku Roma.

22 Pamene anatuma ku Masedoniya awiri a iwo anamtumikira, Timoteo ndi Erasto, iye mwini anakhalabe nthawi mu Asiya.

23 Nthawi yomweyo kunali phokoso lambiri kunena za Njirayo.

24 Pakuti munthu wina dzina lake Demetrio wosula siliva, amene anapanga tiakachisi tasiliva, ta Aritemi, anaonetsera amisiri phindu lambiri;

25 amenewo iye anawasonkhanitsa pamodzi ndi amisiri a ntchito yomweyo, nati, Amuna inu, mudziwa kuti ndi malonda awa ife tipeza chuma chathu.

26 Ndipo muona ndi kumva, kuti si pa Efeso pokha, koma monga pa Asiya ponse, Paulo uyu akopa ndi kutembenutsa anthu ambiri, ndi kuti, Si milungu iyi imene ipangidwa ndi manja:

27 ndipo tiopa ife kuti ntchito yathuyi idzayamba kunyonyosoka; komanso kuti Kachisi wa mulungu wamkazi Aritemi adzayamba kuyesedwa wachabe; ndiponso kuti iye adzayamba kutsitsidwa ku ukulu wake, iye amene a mu Asiya onse, ndi onse a m’dziko lokhalamo anthu, ampembedza.

28 Ndipo pamene anamva, anadzala ndi mkwiyo, nafuula, nati, Wamkulu ndi Aritemi wa ku Efeso.

29 Ndipo m’mzinda monse munachita piringupiringu, nathamangira onse pamodzi ku bwalo losewera, atagwira Gayo ndi Aristariko, anthu a ku Masedoniya, alendo anzake a Paulo.

30 Ndipo pamene Paulo anafuna kulowa kwa anthu, ophunzira ake sanamloleze.

31 Ndipo akulu ena a Asiyanso, popeza anali abwenzi ake, anatumiza mau kwa iye, nampempha asadziponye kubwalo lakusewera.

32 Ndipo ena anafuula kanthu kena, ena kanthu kena; pakuti msonkhanowo unasokonezeka; ndipo unyinji sunadziwe chifukwa chake cha kusonkhana.

33 Ndipo anatulutsa Aleksandro m’khamumo, kumtulutsa iye Ayuda. Ndipo Aleksandro anatambasula dzanja, nafuna kudzikanira kwa anthu adasonkhanawo.

34 Koma pozindikira kuti ali Myuda, kunali mau amodzi a kwa onse akufuula monga maora awiri, Wamkulu ndi Aritemi wa Aefeso.

35 Ndipo pamene mlembi adatontholetsa khamulo, anati, Amuna a Efeso inu, munthuyu ndani wosadziwa kuti mzinda wa Aefeso ndiwo wosungira Kachisi wa Aritemi wamkulu, ndi fano lidachokera kwa Zeusi?

36 Popeza tsono izi sizikanika, muyenera inu kukhala chete, ndi kusachita kanthu kaliuma.

37 Pakuti mwatenga anthu awa, osakhala olanda za mu Kachisi, kapena ochitira mulungu wathu mwano.

38 Ngati tsono Demetrio ndi amisiri okhala naye, ali ndi mlandu ndi munthu, mabwalo a milandu alipo, ndi ziwanga zilipo; anenezane.

39 Koma ngati mufuna kanthu ka zinthu zina, kadzakonzeka m’msonkhano wolamulidwa.

40 Pakutinso palipo potiopsa kuti adzatineneza za chipolowe chalero; popeza palibe chifukwa cha kufotokozera za chipiringu chimene.

41 Ndipo pamene ananena izi, anamasula msonkhano.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ACT/19-733a1e868c0c157ff2d7618d22c6b455.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *