Categories
MACHITIDWE

MACHITIDWE 12

Herode azunza Mpingo; amupha Yakobo, naponya Petro kundende. Petro apulumuka m’ndende. Imfa ya Herode

1 Koma nyengo imeneyoHerodemfumu anathira manja ena a muMpingokuwachitira zoipa.

2 Ndipo adapha ndi lupanga Yakobo mbale wa Yohane.

3 Ndipo pakuona kuti kudakondweretsa Ayuda, anaonjezapo nagwiranso Petro. Ndipo awo ndi masiku a mkate wopanda chotupitsa.

4 Ndipo m’mene adamgwira, anamuika m’ndende, nampereka kwa magulu anai a alonda, lonse anaianai, amdikire iye; ndipo anafuna kumtulutsa kudza naye kwa anthu atapitaPaska.

5 Pamenepo ndipo Petro anasungika m’ndende; koma Mpingo anampempherera iye kwa Mulungu kosalekeza.

6 Ndipo pamene Herode anati amtulutse, usiku womwewo Petro analikugona pakati pa asilikali awiri, womangidwa ndi maunyolo awiri; ndipo alonda akukhala pakhomo anadikira ndende.

7 Ndipo taonani,mngelowa Ambuye anaimirirapo, ndipo kuunika kunawala mokhalamo iye; ndipo anakhoma Petro m’nthiti, namuutsa iye, nanena, Tauka msanga. Ndipo maunyolo anagwa kuchoka m’manja mwake.

8 Ndipo mngelo anati kwa iye, Dzimangire m’chuuno, numange nsapato zako. Nachita chotero. Ndipo ananena naye, Funda chovala chako, nunditsate ine.

9 Ndipo anatuluka, namtsata; ndipo sanadziwe kuti nchoona chochitidwa ndi mngelo, koma anayesa kuti alikuona masomphenya.

10 Ndipo m’mene adapitirira podikira poyamba ndi pachiwiri, anadza kuchitseko chachitsulo chakuyang’ana kumzinda; chimene chidawatsegukira chokha; ndipo anatuluka, napitirira khwalala limodzi; ndipo pomwepo mngelo anamchokera.

11 Ndipo Petro atatsitsimuka, anati, Tsopano ndidziwa zoona, kuti Ambuye anatuma mngelo wake nandilanditsa ine m’dzanja la Herode, ndi ku chilingiriro chonse cha Ayuda.

12 Ndipo m’mene adalingirirapo, anadza kunyumba ya Maria amake wa Yohane wonenedwanso Marko; pamenepo ambiri adasonkhana pamodzi, ndipo analikupemphera.

13 Ndipo m’mene anagogoda pa chitseko cha pakhomo, anadza kudzavomera mdzakazi, dzina lake Roda.

14 Ndipo pozindikira mau ake a Petro, chifukwa cha kukondwera sanatsegule pakhomo, koma anathamanga nalowanso, nawauza kuti Petro alikuima pakhomo.

15 Koma anati kwa iye, Wamisala iwe. Ndipo analimbika ndi kunena kuti nkutero. Ndipo ananena, Ndiye mngelo wake.

16 Koma Petro anakhala chigogodere; ndipo m’mene adamtsegulira, anamuona iye, nadabwa.

17 Koma m’mene adawatambasulira dzanja akhale chete, anawafotokozera umo adamtulutsira Ambuye m’ndende. Ndipo anati, Muwauze Yakobo ndi abale izi. Ndipo anatuluka napita kwina.

18 Koma kutacha, panali phokoso lalikulu mwa asilikali, Petro wamuka kuti.

19 Ndipo pamene Herode adamfunafuna, wosampeza, anafunsitsa odikira nalamulira aphedwe. Ndipo anatsika ku Yudeya kunka ku Kesareya, nakhalabe kumeneko.

20 Koma Herode anaipidwa nao a ku Tiro ndi Sidoni; ndipo anamdzera iye ndi mtima umodzi, ndipo m’mene adakopa Blasito mdindo wa mfumu, anapempha mtendere, popeza dziko lao linapeza zakudya zochokera ku dziko la mfumu.

21 Ndipo tsiku lopangira Herode anavala zovala zachifumu, nakhala pa mpando wachifumu, nawafotokozera iwo mau a pabwalo.

22 Ndipo anthu osonkhanidwawo anafuula, Ndiwo mau a Mulungu, si a munthu ai.

23 Ndipo pomwepo mngelo wa Ambuye anamkantha, chifukwa sanampatse Mulungu ulemerero; ndipo anadyedwa ndi mphutsi, natsirizika.

24 Koma mau a Mulungu anakula, nachulukitsa.

25 Ndipo Barnabasi ndi Saulo anabwera kuchokera kuYerusalemum’mene adatsiriza utumiki wao, natenga Yohane wonenedwanso Marko amuke nao.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ACT/12-2e81b23a94deeabe05ff9ceefbec99c4.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *