Yesu atuma ophunzira ake kukalalikira mau
1 Ndipo Iye anaitana pamodzi khumi ndi awiriwo nawapatsa mphamvu ndi ulamuliro pa ziwanda zonse, ndi zakuchiritsa nthenda.
2 Ndipo anawatuma kukalalikira Ufumu wa Mulungu, ndi kuchiritsa anthu odwala.
3 Ndipo Iye anati kwa iwo, Musanyamule kanthu ka paulendo, kapena ndodo, kapena thumba, kapena mkate, kapena ndalama; ndipo musakhale nao malaya awiri.
4 Ndipo m’nyumba iliyonse mukalowemo, khalani komweko, ndipo muzikachokera kumeneko.
5 Ndipo onse amene sakakulandireni inu, m’mene mutuluka m’mudzi womwewo, sansani fumbi la pa mapazi anu, likhale mboni ya paiwo.
6 Ndipo iwo anatuluka, napita m’midzi yonse, ndi kulalikira Uthenga Wabwino, ndi kuchiritsa ponse.
Herode ndi Yohane Mbatizi
7 NdipoHerodechiwangacho anamva mbiri yake ya zonse zinachitika; ndipo inamthetsa nzeru, chifukwa ananena anthu ena, kuti Yohane anauka kwa akufa;
8 koma ena, kuti Eliya anaoneka; ndipo ena, kutimneneriwina wa akale aja anauka.
9 Ndipo Herode anati, Yohane ndinamdula mutu ine; koma uyu ndani ndikumva zotere za iye? Ndipo anafunafuna kumuona Iye.
Yesu achulukitsa mikate
10 Ndipo atabweraatumwi, anamfotokozera Iye zonse anazichita. Ndipo Iye anawatenga, napatuka nao pa okha kunka kumzinda dzina lake Betsaida.
11 Koma unyinji wa anthu, pamene anadziwa, anamtsata Iye; ndipo Iye anawalandira, nalankhula nao za Ufumu wa Mulungu, nachiritsa amene anasowa kuchiritsidwa.
12 Koma dzuwa lidapendeka; ndipo khumi ndi awiriwo anadza, nati kwa Iye, Tauzani makamu a anthu amuke, kuti apite kumidzi yoyandikira ndi kumadera, kukafuna pogona, ndi kupeza zakudya; chifukwa tili kumalo achipululu kuno.
13 Koma anati kwa iwo, Muwapatse chakudya ndinu. Koma anati, Ife tilibe mikate, koma isanu yokha, ndi nsomba ziwiri zokha; kapena timuke ife kukagulira anthu awa onse zakudya.
14 Pakuti anali amuna ngati zikwi zisanu. Koma Iye anati kwaophunziraake, Khalitsani iwo pansi magulumagulu, ngati makumi asanuasanu.
15 Ndipo anatero, nawakhalitsa pansi onsewo.
16 Ndipo Iye, m’mene anatenga mikate isanu ija ndi nsomba ziwiri anayang’ana kumwamba, nazidalitsa, nanyema, napatsa ophunzira apereke kwa anthuwo.
17 Ndipo anadya, nakhuta onsewo; natola makombo, madengu khumi ndi awiri.
Petro avomereza Khristu
18 Ndipo kunali, pamene Iye anali kupemphera padera, ophunzira anali naye; ndipo anawafunsa iwo, kuti, Makamuwo a anthu anena kuti Ine ndine yani?
19 Ndipo anayankha nati, Yohane Mbatizi; koma ena, Eliya; ndi ena, kuti anauka mmodzi wa aneneri akale.
20 Ndipo anati kwa iwo, Koma inu munena kuti Ine ndine yani? Ndipo anayankha Petro, nati,Khristuwa Mulungu.
21 Ndipo Iye anawauzitsa iwo, nalamulira kuti asanene ichi kwa munthu aliyense;
22 nati, Kuyenera kutiMwana wa Munthuamve zowawa zambiri, ndi kukanidwa ndi akulu, ndi ansembe aakulu, ndi alembi, ndi kuphedwa, ndi kuuka tsiku lachitatu.
Za kusenza mtanda
23 Ndipo Iye ananena kwa onse, Ngati munthu afuna kudza pambuyo panga, adzikanize yekha, nanyamule mtanda wake tsiku ndi tsiku, nanditsate Ine.
24 Pakuti aliyense amene akafuna kupulumutsa moyo wake, iye adzautaya; koma aliyense amene akataya moyo wake chifukwa cha Ine, iye adzaupulumutsa uwu.
25 Pakuti munthu apindulanji, akadzilemezera dziko lonse lapansi nadzitayapo, kapena kulipapo moyo wake?
26 Pakuti aliyense amene adzachita manyazi chifukwa cha Ine ndi mau anga, Mwana wa Munthu adzachita manyazi chifukwa cha iye, pamene adzafika ndi ulemerero wake ndi wa Atate, ndi waangelooyera.
27 Koma Ine ndinena ndi inu zoonadi, Kuli ena a iwo akuimirira pano, amene sadzalawatu imfa, kufikira kuti adzaona Ufumu wa Mulungu.
Mawalitsidwe a Yesu paphiri
28 Ndipo pamene padatha ngati masiku asanu ndi atatu atanena mau amenewa, Iye anatenga Petro ndi Yohane ndi Yakobo apite naye, nakwera m’phiri kukapemphera.
29 Ndipo m’kupemphera kwake, maonekedwe a nkhope yake anasandulika, ndi chovala chake chinayera ndi kunyezimira.
30 Ndipo onani, analikulankhulana naye amuna awiri, ndiwo Mose ndi Eliya;
31 amene anaonekera mu ulemerero, nanena za kumuka kwake kumene Iye ati adzatsiriza kuYerusalemu.
32 Koma Petro ndi iwo anali naye analemedwa ndi tulo; koma m’mene anayera m’maso ndithu, anaona ulemerero wake, ndi amuna awiriwo akuimirira ndi Iye.
33 Ndipo panali polekana iwo aja ndi Iye, Petro anati kwa Yesu, Ambuye, nkwabwino kuti tili pano; ndipo timange misasa itatu, umodzi wa Inu, ndi wina wa Mose, ndi wina wa Eliya; wosadziwa iye chimene alikunena.
34 Ndipo akadalankhula izi, unadza mtambo, nuwaphimba iwo; ndipo anaopa pakulowa iwo mumtambo.
35 Ndipo munatuluka mau mumtambo, nanena, Uyu ndiye Mwana wanga, wosankhidwayo; mverani Iye.
36 Ndipo pakutero mauwo, Yesu anapezedwa ali yekha. Ndipo iwo anakhala chete, ndipo sanauze munthu aliyense masiku aja kanthu konse ka izo anaziona.
Achiritsa mwana wodwala khunyu
37 Ndipo panali, m’mawa mwake, atatsika m’phiri, khamu lalikulu la anthu linakomana naye.
38 Ndipo onani, anafuula munthu wa m’khamulo, nanena, nati, Mphunzitsi, ndikupemphani, yang’anirani mwana wanga; chifukwa ndiye mmodzi yekha wa ine:
39 ndipo onani, umamgwira iye mzimu, nafuula modzidzimuka; ndipo umamng’amba iye ndi kumchititsa thovu pakamwa, suchoka pa iye, koma umsautsa koopsa.
40 Ndipo ndinapempha ophunzira anu kuti autulutse; koma sanathe.
41 Ndipo Yesu anayankha, nati, Ha! Obadwa inu osakhulupirira ndi amphulupulu, ndidzakhala ndi inu nthawi yanji, ndi kulekerera inu? Idza naye kuno mwana wako.
42 Ndipo akadadza iye, chiwandacho chinamgwetsa, ndi kumng’ambitsa. Koma Yesu anadzudzula mzimu wonyansawo, nachiritsa mnyamata, nambwezera iye kwa atate wake.
43 Ndipo onse anadabwa pa ukulu wake wa Mulungu. Koma pamene onse analikuzizwa ndi zonse anazichita, Iye anati kwa ophunzira ake,
44 Alowe mau amenewa m’makutu anu; pakuti Mwana wa Munthu adzaperekedwa m’manja a anthu.
45 Koma iwo sanadziwitse mau awa, ndipo anabisidwa kwa iwo, kuti asawadziwe; ndipo anaopa kumfunsa za mau awa.
Wamkulu mu Ufumu wa Kumwamba
46 Ndipo anayamba kutsutsana kuti wamkulu mwa iwo ndani.
47 Koma Yesu pakuona kutsutsana kwa mitima yao, anatenga kamwana, nakaimika pambali pake, nati kwa iwo,
48 Amene aliyense akalandire kamwana aka m’dzina langa alandira Ine; ndipo amene andilandira Ine alandira Iye amene anandituma Ine; pakuti iye wakukhala wamng’onong’ono wa inu nonse, yemweyu ndiye wamkulu.
Osatsutsana nafe athandizana nafe
49 Ndipo Yohane anayankha nati, Ambuye, tinaona wina alikutulutsa ziwanda m’dzina lanu; ndipo tinamletsa, chifukwa satsatana nafe.
50 Koma Yesu anati kwa iye, Musamletse, pakuti iye amene satsutsana nanu athandizana nanu.
Asamariya amkaniza Yesu
51 Ndipo panali, pamene anayamba kukwanira masiku akuti alandiridwe Iye kumwamba, Yesu anatsimikiza kuloza nkhope yake kunka ku Yerusalemu,
52 natumiza amithenga patsogolo pake; ndipo ananka, nalowa m’mudzi waAsamariya, kukamkonzera Iye malo.
53 Ndipo iwo sanamlandire Iye, chifukwa nkhope yake inali yoloza kunka ku Yerusalemu.
54 Ndipo pamene ophunzira ake Yakobo ndi Yohane anaona, anati, Ambuye, Kodi mufuna kuti ife tiuze moto utsike kumwamba ndi kuwanyeketsa iwo?
55 Koma Iye anapotoloka nawadzudzula.
56 Ndipo anapita kumudzi kwina.
Matsatidwe a Yesu
57 Ndipo m’mene iwo analikuyenda m’njira, munthu anati kwa Iye, Ine ndidzakutsatani kumene kulikonse mukapitako.
58 Ndipo Yesu anati kwa iye, Nkhandwe zili nazo nkhwimba, ndi mbalame za kumwamba zisa, koma Mwana wa Munthu alibe potsamira mutu.
59 Ndipo anati kwa munthu wina, Unditsate Ine. Koma iye anati, Mundilole ine, Ambuye, ndiyambe ndamuka kuika maliro a atate wanga.
60 Koma anati kwa iye, Leka akufa aike akufa a eni okha; koma muka iwe nubukitse mbiri yake ya Ufumu wa Mulungu.
61 Ndipo winanso anati, Ambuye ndidzakutsatani Inu; koma muyambe mwandilola kulawirana nao a kunyumba kwanga.
62 Koma Yesu anati kwa iye, Palibe munthu wakugwira chikhasu, nayang’ana za kumbuyo, ayenera Ufumu wa Mulungu.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/LUK/9-99296c912029fd5fc8bb7bc77ff750ff.mp3?version_id=1068—