Categories
LUKA

LUKA 3

Kulalikira kwa Yohane Mbatizi

1 Ndipo pa chaka chakhumi ndi chisanu cha ufumu wa TiberioKaisara, pokhala Pontio Pilato kazembe wa Yudeya, ndiHerodechiwanga cha Galileya, ndi Filipo mbale wake chiwanga cha dziko la Itureya ndi la Trakoniti, ndi Lisaniasi chiwanga cha Abilene;

2 pa ukulu wansembe wao wa Anasi ndi Kayafa, panadza mau a Mulungu kwa Yohane mwana wa Zekariya m’chipululu.

3 Ndipo iye anadza kudziko lonse la m’mbali mwa Yordani, nalalikira ubatizo wa kulapa mtima kuloza ku chikhululukiro cha machimo;

4 monga mwalembedwa m’buku la Yesayamneneri, kuti,

Mau a wofuula m’chipululu,

konzani khwalala la Ambuye,

lungamitsani njira zake.

5 Chigwa chilichonse chidzadzazidwa,

ndipo phiri lililonse ndi mtunda uliwonse zidzachepsedwa;

ndipo zokhota zidzakhala zolungama,

ndipo njira za zigoloondo zidzakhala zosalala;

6 ndipo anthu onse adzaona chipulumutso cha Mulungu.

7 Chifukwa chake iye ananena kwa makamuwo a anthu amene anatulukira kukabatizidwa ndi iye, Obadwa a njoka inu, anakulangizani inu ndani kuthawa mkwiyo ulinkudza?

8 Chifukwa chake balani zipatso zakuyenera kulapa mtima, ndipo musayambe kunena mwa inu nokha, Atate wathu tili naye ndiye Abrahamu: pakuti ndinena kwa inu, kuti ali ndi mphamvu Mulungu, mwa miyala iyi, kuukitsira Abrahamu ana.

9 Ndiponso tsopano lino nkhwangwa yaikidwa pa mizu ya mitengo; chotero mtengo uliwonse wosabala chipatso chabwino udulidwa, nuponyedwa pamoto.

10 Ndipo anthu a makamu anamfunsa iye, nanena, Ndipo tsono tizichita chiyani?

11 Koma iye anayankha nanena kwa iwo, Iye amene ali nao malaya awiri apatse kwa iye amene alibe; ndi iye amene ali nazo zakudya achite chomwecho.

12 Ndipoamisonkhoomwe anadza kudzabatizidwa, nati kwa iye, Mphunzitsi, ife tizichita chiyani?

13 Koma iye anati kwa iwo, Musakapambe kanthu konse kakuposa chimene anakulamulirani.

14 Ndipo asilikali omwe anamfunsa iye, nati, Nanga ife tizichita chiyani? Ndipo iye anati kwa iwo, Musaopse, musanamize munthu aliyense; khalani okhuta ndi kulipira kwanu.

15 Ndipo pamene anthu anali kuyembekezera, ndipo onse anaganizaganiza m’mitima yao za Yohane, ngati kapena iye aliKhristu;

16 Yohane anayankha, nanena kwa onse, Inetu ndikubatizani inu ndi madzi; koma wakundiposa ine mphamvu alinkudza, amene sindiyenera kumasula zingwe za nsapato zake; Iyeyu adzakubatizani inu ndi Mzimu Woyera ndi moto:

17 amene chouluzira chake chili m’dzanja lake, kuti ayeretse padwale pake, ndi kusonkhanitsa tirigu m’nkhokwe yake; koma mankhusu adzatentha m’moto wosazima.

18 Choteretu iye anauza anthu Uthenga Wabwino ndi kuwadandaulira zinthu zina zambiri.

19 KomaHerodemfumu ija, m’mene Yohane anamdzudzula chifukwa cha Herodiasi, mkazi wa mbale wake, ndi cha zinthu zonse zoipa Herode anazichita,

20 anaonjeza pa zonsezi ichinso, kuti anatsekera Yohane m’nyumba yandende.

Yesu abatizidwa

21 Pamene anthu onse anabatizidwa, Yesu nayenso anabatizidwa. Iye anali kupemphera, ndipo kuthambo kunatseguka,

22 ndipo Mzimu Woyera anatsika ndi maonekedwe a thupi lake ngati nkhunda, nadza pa Iye; ndipo munatuluka mau m’thambo, kuti, Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa, mwa Iwe ndikondwera.

Makolo a Yesu

23 Ndipo Yesuyo, pamene anayamba ntchito yake, anali monga wa zaka makumi atatu, ndiye (monga anthu adamuyesa) mwana wa Yosefe, mwana wa Eli,

24 mwana wa Matati, mwana wa Levi, mwana wa Meliki, mwana wa Yanai, mwana wa Yosefe,

25 mwana wa Matatiasi, mwana wa Amosi, mwana wa Nahumu, mwana wa Hesili, mwana wa Nagai,

26 mwana wa Mahati, mwana wa Matatiasi, mwana wa Semeini, mwana wa Yoseke, mwana wa Yoda,

27 mwana wa Yohanani, mwana wa Resa, mwana wa Zerubabele, mwana wa Sealatiele, mwana wa Neri,

28 mwana wa Meliki, mwana wa Adi, mwana wa Kosamu, mwana wa Elimadama, mwana wa Eri,

29 mwana wa Yose, mwana wa Eliyezere, mwana wa Yorimu, mwana wa Matati, mwana wa Levi,

30 mwana wa Simeoni, mwana wa Yudasi, mwana wa Yosefe, mwana wa Yonamu, mwana wa Eliyakimu,

31 mwana wa Melea, mwana wa Mena, mwana wa Matata, mwana wa Natamu, mwana wa Davide,

32 mwana wa Yese, mwana wa Obede, mwana wa Bowazi, mwana wa Salimoni, mwana wa Nasoni,

33 mwana wa Aminadabu, mwana wa Admini, mwana wa Arini, mwana wa Hezironi, mwana wa Perezi, mwana wa Yuda,

34 mwana wa Yakobo, mwana wa Isaki, mwana wa Abrahamu, mwana wa Tera, mwana wa Nahori,

35 mwana wa Serugi, mwana wa Reu, mwana wa Pelegi, mwana wa Eberi, mwana wa Sela,

36 mwana wa Kainani, mwana wa Arifaksadi, mwana wa Semu, mwana wa Nowa, mwana wa Lameki,

37 mwana wa Metusela, mwana wa Enoki, mwana wa Yaredi, mwana wa Mahalalele, mwana wa Kainani,

38 mwana wa Enosi, mwana wa Seti, mwana waAdamu, mwana wa Mulungu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/LUK/3-1e8865de12b328f436ba6493d1c9c9ea.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *