Mphatso ya mkazi wamasiye
1 Ndipo Yesu anakweza maso, naona anthu eni chuma alikuika zopereka zao mosungiramo ndalama.
2 Ndipo anaona mkazi wina wamasiye waumphawi alikuika momwemo timakobiri tiwiri.
3 Ndipo Iye anati, Zoonadi ndinena kwa inu, wamasiye uyu waumphawi anaikamo koposa onse;
4 pakuti onse amenewa anaika mwa unyinji wao pa zoperekazo; koma iye mwa kusowa kwake anaikamo za moyo wake, zonse anali nazo.
Yesu aneneratu zam’tsogolo, chiyambi cha masautso
5 Ndipo pamene ena analikunena za Kachisiyo, kuti anakonzeka ndi miyala yokoma ndi zopereka, anati Iye,
6 Zinthu izi muziona, adzafika masiku, pamenepo sudzasiyidwa pano mwala pamwala unzake, umene sudzagwetsedwa.
7 Ndipo iwo anamfunsa Iye, nati, Mphunzitsi, nanga zinthu izi zidzaoneka liti? Ndipo chizindikiro ndi chiyani pamene izi ziti zichitike?
8 Ndipo Iye anati, Yang’anirani musasocheretsedwe; pakuti ambiri adzadza m’dzina langa, nadzanena, Ndine amene; ndipo, Nthawi yayandikira; musawatsate pambuyo pao.
9 Ndipo pamene mudzamva za nkhondo ndi mapanduko, musaopsedwa; pakuti ziyenera izi ziyambe kuchitika; koma mathedwe sakhala pomwepo.
10 Pamenepo ananena nao, Mtundu wa anthu udzaukira pa mtundu wina, ndipo ufumu pa ufumu wina:
11 ndipo kudzakhala zivomezi zazikulu, ndi njala ndi miliri m’malo akutiakuti, ndipo kudzakhala zoopsa ndi zizindikiro zazikulu zakumwamba.
12 Koma zisanachitike izi, anthu adzakuthirani manja, nadzakuzunzani, nadzapereka inu ku masunagogendi ndende, nadzamuka nanu kwa mafumu ndi akazembe, chifukwa cha dzina langa.
13 Kudzakhala kwa inu ngati umboni.
14 Chifukwa chake tsimikizani mumtima mwanu, kuti usanafike mlandu musalingirire chimene mudzayankha.
15 Pakuti Ine ndidzakupatsani inu kamwa ndi nzeru, zimene adani anu onse sadzatha kuzikana kapena kuzitsutsa.
16 Koma mudzaperekedwa ngakhale ndi akukubalani, ndi abale, ndi a fuko lanu, ndi abwenzi anu; ndipo ena a inu adzakuphani.
17 Ndipo anthu onse adzadana ndi inu chifukwa cha dzina langa.
18 Ndipo silidzaonongeka tsitsi limodzi la pamutu panu.
19 Mudzakhala nao moyo wanu m’chipiriro.
Aneneratu za kupasuka kwa Yerusalemu
20 Koma pamene paliponse mudzaonaYerusalemuatazingidwa ndi magulu a ankhondo, zindikirani pamenepo kuti chipulumutso chake chayandikira.
21 Pamenepo iwo ali mu Yudeya athawire kumapiri, ndi iwo ali m’kati mwa uwo atuluke, ndi iwo ali kuminda asalowemo.
22 Chifukwa amenewa ndi masiku akubwezera, kuti zonse zidalembedwa zichitike.
23 Koma tsoka iwo akukhala ndi pakati, ndi iwo akuyamwitsa ana masiku awo! Pakuti padzakhala chisauko chachikulu padziko, ndi mkwiyo pa anthu awa.
24 Ndipo adzagwa ndi lupanga lakuthwa, nadzagwidwa ndende kunka kumitundu yonse ya anthu; ndipo mapazi a anthu akunja adzapondereza Yerusalemu kufikira kuti nthawi zao za anthu akunja zakwanira.
Za kubwera kwa Mwana wamunthu
25 Ndipo kudzakhala zizindikiro pa dzuwa ndi mwezi ndi nyenyezi; ndi padziko lapansi chisauko cha mitundu ya anthu, alikuthedwa nzeru pa mkokomo wake wa nyanja ndi mafunde ake;
26 anthu akukomoka ndi mantha, ndi kuyembekezera zinthu zilinkudza kudziko lapansi; pakuti mphamvu zakumwamba zidzagwedezeka.
27 Ndipo pamenepo adzaonaMwana wa Munthualinkudza mu mtambo ndi mphamvu ndi ulemerero waukulu.
28 Koma poyamba kuchitika izi weramukani, tukulani mitu yanu; chifukwa chiomboledwe chanu chayandikira.
29 Ndipo ananena naofanizo; Onani mkuyu, ndi mitengo yonse:
30 pamene iphukira, muipenya nimuzindikira pa nokha kuti dzinja lili pafupi pomwepo.
31 Inde chotero inunso, pakuona zinthu izi zilikuchitika, zindikirani kuti Ufumu wa Mulungu uli pafupi.
32 Indetu ndinena ndinu, Mbadwo uno sudzapitirira, kufikira zonse zitachitika.
33 Thambo ndi dziko lapansi zidzapita; koma mau anga sadzapita.
Khalani odikira
34 Koma mudziyang’anire nokha, kuti kapena mitima yanu ingalemetsedwe ndi madyaidya ndi kuledzera, ndi zosamalira za moyo uno, ndi kuti tsiku ilo lingafikire inu modzidzimutsa ngati msampha;
35 pakuti lidzatero ndi kufikira anthu onse akukhala pankhope padziko lonse lapansi.
36 Koma inu dikirani nyengo zonse, ndi kupemphera, kuti mukalimbike kupulumuka zonse zimene zidzachitika, ndi kuimirira pamaso pa Mwana wa Munthu.
37 Ndipo usana uliwonse Iye analikuphunzitsa mu Kachisi; ndi usiku uliwonse anatuluka, nagona paphiri lotchedwa la Azitona.
38 Ndipo anthu onse analawira mamawa kudza kwa Iye ku Kachisi kudzamvera Iye.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/LUK/21-6cdd412e4786b255e8ee01d3237fd43c.mp3?version_id=1068—