Categories
LUKA

LUKA 2

Kubadwa kwa Yesu Khristu

1 Ndipo kunali masiku aja, kuti lamulo linatuluka kwaKaisaraAugusto kuti dziko lonse lokhalamo anthu lilembedwe;

2 ndiko kulembera koyamba pokhala Kwirinio kazembe wa Siriya.

3 Ndipo onse anamuka kulembedwa, munthu aliyense kumzinda wake.

4 Ndipo Yosefe yemwe anakwera kuchokera ku Galileya, kumzinda wa Nazarete, kunka ku Yudeya, kumzinda wa Davide, dzina lake Betelehemu, chifukwa iye anali wa banja ndi fuko lake la Davide;

5 kukalembedwa iye mwini pamodzi ndi Maria, wopalidwa naye ubwenzi; ndi uyu anali ndi pakati.

6 Ndipo panali pokhala iwo komweko, masiku ake a kubala anakwanira.

7 Ndipo iye anabala mwana wake wamwamuna woyamba; namkulunga Iye m’nsalu, namgoneka modyera ng’ombe, chifukwa kuti anasowa malo m’nyumba ya alendo.

Abusa a ku Betelehemu

8 Ndipo panali abusa m’dziko lomwelo, okhala kubusa ndi kuyang’anira zoweta zao usiku.

9 Ndipomngelowa Ambuye anaimirira pa awo, ndi kuwala kwa Ambuye kunawaunikira kozungulira: ndipo anaopa ndi mantha aakulu.

10 Ndipo mngelo anati kwa iwo, Musaope; pakuti onani, ndikuuzani inu uthenga wabwino wa chikondwero chachikulu, chimene chidzakhala kwa anthu onse;

11 pakuti wakubadwirani inu lero, m’mzinda wa Davide, Mpulumutsi, amene aliKhristuAmbuye.

12 Ndipo ichi ndi chizindikiro kwa inu: Mudzapeza mwana wakhanda wokuta ndi nsalu atagona modyera.

13 Ndipo dzidzidzi panali pamodzi ndi mngeloyo ambirimbiri a gulu la Kumwamba, natamanda Mulungu, nanena,

14 Ulemerero ukhale kwa Mulungu Kumwambamwamba,

ndi mtendere pansi pano mwa anthu amene akondwera nao.

15 Ndipo panali, pamene angelo anachokera kwa iwo kunka Kumwamba, abusa anati wina ndi mnzake, Tipitiretu ku Betelehemu, tikaone chinthu ichi chidachitika, chimene Ambuye anatidziwitsira ife.

16 Ndipo iwo anadza ndi changu, napeza Maria, ndi Yosefe, ndi mwana wakhanda atagona modyera.

17 Ndipo iwo, m’mene anaona, anadziwitsa anthu za mau analankhulidwa kwa iwo a mwana uyu.

18 Ndipo anthu onse amene anamva anazizwa ndi zinthu abusa adalankhula nao.

19 Koma Maria anasunga mau awa onse, nawalingalira mumtima mwake.

20 Ndipo abusawo anabwera, nalemekeza ndi kutamanda Mulungu pa zinthu zonse anazimva, naziona, monga kunalankhulidwa kwa iwo.

Kudulidwa ndi kuperekedwa kwa Yesu

21 Ndipo pamene panakwanira masiku asanu ndi atatu akumdula Iye, anamutcha dzina lake Yesu, limene anatchula mngeloyo asanalandiridwe Iye m’mimba.

22 Ndipo pamene anakwanira masiku a kukonza kwao, monga mwa chilamulo cha Mose, iwo anakwera naye kunka kuYerusalemu, kukamsonyeza Iye kwa Ambuye,

23 (monga mwalembedwa m’chilamulo cha Ambuye, kuti mwamuna aliyense wotsegula pa mimba ya amake adzanenedwa wopatulika wa kwa Ambuye)

24 ndi kukapereka nsembe monga mwanenedwa m’chilamulo cha Ambuye, njiwa ziwiri, kapena maunda awiri.

Za Simeoni ndi za Anna

25 Ndipo onani, mu Yerusalemu munali munthu, dzina lake Simeoni; ndipo munthu uyu, wolungama mtima ndi wopemphera, analikulindira matonthozedwe a Israele; ndipo Mzimu Woyera anali pa iye.

26 Ndipo anamuululira Mzimu Woyera kuti sadzaona imfa, kufikira adzaona Khristu wake wa Ambuye.

27 Ndipo iye analowa ku Kachisi ndi Mzimu: ndipo pamene atate ndi amake analowa ndi kamwanako Yesu, kudzamchitira Iye mwambo wa chilamulo,

28 pomwepo iye anamlandira Iye m’manja mwake, nalemekeza Mulungu, nati,

29 Tsopano, Ambuye, monga mwa mau anu aja,

lolani ine, kapolo wanu, ndichoke mumtendere;

30 chifukwa maso anga adaona chipulumutso chanu,

31 chimene munakonza pamaso pa anthu onse,

32 kuunika kukhale chivumbulutso cha kwa anthu a mitundu,

ndi ulemerero wa anthu anu Israele.

33 Ndipo atate ndi amake anali kuzizwa ndi zinthu zolankhulidwa za Iye.

34 Ndipo Simeoni anawadalitsa, nati kwa Maria amake, Taona, Uyu waikidwa akhale kugwa ndi kunyamuka kwa anthu ambiri mwa Israele; ndipo akhale chizindikiro chakutsutsana nacho;

35 eya, ndipo lupanga lidzakupyoza iwe moyo wako; kuti maganizo a m’mitima yambiri akaululidwe.

36 Ndipo panali Anna,mneneriwamkazi, mwana wa Fanuwele, wa fuko la Asere; amene anali wokalamba ndithu, nakhala ndi mwamuna wake, kuyambira pa unamwali wake,

37 zaka zisanu ndi ziwiri, ndipo anali wamasiye wa kufikira zaka zake makumi asanu ndi atatu mphambu zinai, amene sankachoka ku Kachisi, wotumikira Mulungu ndikusala kudyandi kupemphera usiku ndi usana.

38 Ndipo iye anafikako pa nthawi yomweyo, navomerezanso kutama Mulungu, nalankhula za Iye kwa anthu onse akuyembekeza chiombolo cha Yerusalemu.

39 Ndipo pamene iwo anatha zonse monga mwa chilamulo cha Ambuye, anabwera ku Galileya, kumzinda kwao, ku Nazarete.

40 Ndipo mwanayo anakula nalimbika, nalikudzala ndi nzeru; ndi chisomo cha Mulungu chinali pa Iye.

Mnyamata Yesu pakati pa aphunzitsi

41 Ndipo atate wake ndi amake akamuka chaka ndi chaka ku Yerusalemu kuPaska.

42 Ndipo pamene Iye anakhala ndi zaka zake khumi ndi ziwiri, anakwera iwo monga machitidwe a chikondwerero;

43 ndipo pakumaliza masiku ake, pakubwera iwo, mnyamatayo Yesu anatsala m’mbuyo ku Yerusalemu. Ndipo atate ndi amake sanadziwe;

44 koma iwo anayesa kuti Iye ali m’chipiringu cha ulendo, nayenda ulendo wa tsiku limodzi; ndipo anayamba kumfunafuna Iye mwa abale ao ndi mwa anansi ao;

45 ndipo pamene sanampeze, anabwera ku Yerusalemu, namfunafuna Iye.

46 Ndipo pakupita masiku atatu, anampeza Iye mu Kachisi, analikukhala pakati pa aphunzitsi, namva iwo, nawafunsanso mafunso.

47 Ndipo onse amene anamva Iye anadabwa ndi chidziwitso chake, ndi mayankho ake.

48 Ndipo m’mene anamuona Iye, anadabwa; ndipo amake anati kwa Iye, Mwanawe, wachitiranji ife chotero; taona, atate wako ndi ine tinalikufunafuna Iwe ndi kuda nkhawa.

49 Ndipo Iye anati kwa iwo, Kuli bwanji kuti munalikundifunafuna Ine? Simunadziwa kodi kuti kundiyenera Ine ndikhale m’zake za Atate wanga?

50 Ndipo sanadziwitse mau amene Iye analankhula nao.

51 Ndipo anatsika nao pamodzi nadza ku Nazarete; nawamvera iwo: ndipo amake anasunga zinthu izi zonse mumtima mwake.

52 Ndipo Yesu anakulabe m’nzeru ndi mumsinkhu, ndi m’chisomo cha pa Mulungu ndi cha pa anthu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/LUK/2-013093f3a1226e51e733da965eae0be0.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *