Categories
LUKA

LUKA 19

Zakeyo asandulika mtima

1 Ndipo analowa, napyola pa Yeriko.

2 Ndipo taonani, mwamuna wotchedwa dzina lake Zakeyo; ndipo iye anali mkulu waamisonkho, nali wachuma.

3 Ndipo anafuna kuona Yesu ndiye uti, ndipo sanathe, chifukwa cha khamulo, pakuti anali wamfupi msinkhu.

4 Ndipo anathamanga, natsogola, nakwera mumkuyu kukamuona Iye; pakuti anati apite njira yomweyi.

5 Ndipo m’mene anadza pamalopo Yesu anakweza maso nati kwa iye, Zakeyo, fulumira, nutsike; pakuti lero ndiyenera kukhala m’nyumba mwako.

6 Ndipo anafulumira, natsika, namlandira Iye wokondwera.

7 Ndipo m’mene anachiona anadandaula onse, nanena, Analowa amchereze munthu ali wochimwa.

8 Ndipo Zakeyo anaimirira nati kwa Ambuye, Taonani, Ambuye, gawo limodzi la zanga zonse zogawika pakati ndipatsa osauka; ndipo ngati ndalanda kanthu kwa munthu monyenga, ndimbwezera kanai.

9 Ndipo Yesu anati kwa iye, Lero chipulumutso chagwera nyumba iyi, popeza iyenso ndiye mwana wa Abrahamu.

10 PakutiMwana wa Munthuanadza kufunafuna ndi kupulumutsa chotayikacho.

Fanizo la ndalama khumi za mina

11 Ndipo pakumva izi iwo, Iye anaonjeza nanenafanizo, chifukwa anali Iye pafupi paYerusalemu, ndipo iwo anayesa kuti Ufumu wa Mulungu ukuti uonekere pomwepo.

12 Pamenepo anati, Munthu wa fuko lomveka ananka kudziko lakutali, kudzilandirira yekha ufumu, ndi kubwerako.

13 Ndipo anaitana akapolo ake khumi, nawapatsa iwo ndalama khumi za mina, nati kwaiwo, Chita nazoni malonda kufikira ndibweranso.

14 Koma mfulu za pamudzi pake zinamuda, nkutuma akazembe amtsate m’mbuyo ndi kunena, Ife sitifuna munthuyo akhale mfumu yathu.

15 Ndipo kunali, pakubwera iye, atalandira ufumuwo, anati aitanidwe kwa iye akapolo aja, amene adawapatsa ndalamazo, kuti adziwe umo anapindulira pochita malonda.

16 Ndipo anafika woyamba, nanena, Mbuye, mina yanu inachita nionjeza mina khumi.

17 Ndipo anati kwa iye, Chabwino, kapolo wabwino iwe; popeza unakhala wokhulupirika m’chaching’onong’ono, khala nao ulamuliro pa mizinda khumi.

18 Ndipo anadza wachiwiri, nanena, Mbuye, mina yanu yapindula mina zisanu.

19 Ndipo anati kwa iyenso, Khala iwenso woweruza mizinda isanu.

20 Ndipo wina anadza, nanena, Mbuye, taonani, siyi mina yanu, ndaisunga m’kansalu;

21 pakuti ndinakuopani, popeza inu ndinu munthu wouma mtima: munyamula chimene simunachiike pansi, mututa chimene simunachifese.

22 Ananena kwa iye, Pakamwa pako ndikuweruza, kapolo woipa iwe. Unadziwa kuti ine ndine munthu wouma mtima, wonyamula chimene sindinachiike, ndi wotuta chimene sindinachifese;

23 ndipo sunapereke bwanji ndalama yanga pokongoletsa, ndipo ine pakudza ndikadaitenga ndi phindu lake?

24 Ndipo anati kwa iwo akuimirirapo, Mchotsereni minayo, nimuipatse kwa iye wakukhala nazo mina khumi.

25 Ndipo anati kwa iye, Mbuye, ali nazo mina khumi.

26 Ndinena ndi inu, kuti kwa yense wakukhala nacho kudzapatsidwa; koma kwa iye amene alibe kanthu, chingakhale chimene ali nacho chidzachotsedwa.

27 Koma adani anga aja osafuna kuti ndidzakhala mfumu yao, bwerani nao kuno, nimuwaphe pamaso panga.

28 Ndipo m’mene adanena izi anawatsogolera nakwera ku Yerusalemu.

Yesu alowa mu Yerusalemu

29 Ndipo kunali, m’mene anayandikira ku Betefage ndi Betaniya, paphiri lotchedwa la Azitona, anatuma awiri aophunzira,

30 nati, Mukani kumudzi uli pandunji panu; m’menemo, polowa, mudzapeza mwana wa bulu womangidwa, pamenepo palibe munthu anakwerapo nthawi iliyonse; mummasule iye nimumtenge.

31 Ndipo munthu akati kwa inu, Mummasuliranji? Mudzatero naye, Ambuye amfuna iye.

32 Ndipo anachoka otumidwawo, napeza monga adanena kwa iwo.

33 Ndipo pamene anamasula mwana wa bulu, eni ake anati kwa iwo, Mumasuliranji mwana wa bulu?

34 Ndipo anati, Ambuye amfuna iye.

35 Ndipo anadza naye kwa Yesu; ndipo anayalika zovala zao pa mwana wa buluyo, nakwezapo Yesu.

36 Ndipo pakupita Iye, anayala zovala zao m’njira.

37 Ndipo pakuyandikira Iye tsono potsetsereka pake paphiri la Azitona, unyinji wonse wa ophunzira anayamba kukondwera ndi kuyamika Mulungu ndi mau aakulu, chifukwa cha ntchito zonse zamphamvu anaziona;

38 nanena, Wolemekezeka Mfumuyo ikudza m’dzina la Ambuye; mtendere mu Mwamba, ndi ulemerero mu Mwambamwamba.

39 NdipoAfarisiena a m’khamu la anthu anati kwa Iye, Mphunzitsi, dzudzulani ophunzira anu.

40 Ndipo anayankha nati, Ndinena ndi inu, ngati awa khala chete miyala idzafuula.

Yesu alirira Yerusalemu

41 Ndipo m’mene anayandikira, anaona mzindawo naulirira,

42 nanena, Ukadazindikira tsiku ili, inde iwetu zinthu za mtendere! Koma tsopano zibisika pamaso pako.

43 Pakuti masiku adzakudzera, ndipo adani ako adzakuzingira linga, nadzakuzungulira iwe kwete, nadzakutsekereza ponsepo;

44 ndipo adzakupasula iwe, ndi ana ako mwa iwe; ndipo sadzasiya mwa iwe mwala wina pamwala unzake; popeza sunazindikire nyengo ya mayang’aniridwe ako.

Ayeretsa Kachisi kachiwiri

45 Ndipo analowa mu Kachisi, nayamba kutulutsa iwo akugulitsa malonda, nanena nao,

46 Kwalembedwa, Ndipo nyumba yanga idzakhala nyumba yakupemphera; koma inu mwaiyesa phanga la achifwamba.

47 Ndipo analikuphunzitsa mu Kachisi tsiku ndi tsiku. Koma ansembe aakulu, ndi alembi ndi akulu a anthu anafunafuna kumuononga Iye;

48 ndipo sanapeze chimene akachita; pakuti anthu onse anamlendewera Iye kuti amve.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/LUK/19-8a7e45abc844a3dc5a178076f8bd17a8.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *