Fanizo la woweruza wosalungama
1 Ndipo anawanenerafanizolakuti ayenera iwo kupemphera nthawi zonse, osafooka mtima;
2 nanena, M’mzinda mwakuti munali woweruza wosaopa Mulungu, ndi wosasamala munthu.
3 Ndipo m’mzinda momwemo munali mkazi wamasiye; ndipo anadza kwa iye nanena, Mundiweruzire mlandu pa wotsutsana nane.
4 Ndipo sanafune nthawi; koma bwinobwino anati mwa yekha, Ndingakhale sindiopa Mulungu kapena kusamala munthu;
5 koma chifukwa cha kundivuta ine mkazi wamasiye amene ndidzamweruzira mlandu, kuti angandilemetse ndi kudzaidza kwake.
6 Ndipo Ambuye anati, Tamverani chonena woweruza wosalungama.
7 Ndipo kodi Mulungu sadzachitira chilungamo osankhidwa ake akumuitana usana ndi usiku, popeza aleza nao mtima?
8 Ndinena ndi inu, adzawachitira chilungamo posachedwa. KomaMwana wa Munthupakudza Iye, adzapeza chikhulupiriro padziko lapansi kodi?
Fanizo la Mfarisi ndi wamsonkho
9 Ndipo anatinso kwa ena amene anadzikhulupirira mwa iwo okha kuti ali olungama, napeputsa onse ena, fanizo ili,
10 Anthu awiri anakwera kunka ku Kachisi kukapemphera; winayoMfarisindi mnzakewamsonkho.
11 Mfarisiyo anaimirira napemphera izi mwa yekha,Mulungu, ndikuyamikani kuti sindili monga anthu onse ena, opambapamba, osalungama, achigololo, kapenanso monga wamsonkho uyu;
12 ndisala chakudya kawiri sabata limodzi; ndipereka limodzi la magawo khumi la zonse ndili nazo.
13 Koma wamsonkhoyo alikuima patali sanafune kungakhale kukweza maso kumwamba, komatu anadziguguda pachifuwa pake nanena, Mulungu, mundichitire chifundo, ine wochimwa.
14 Ndinena ndi inu, anatsikira kunyumba kwake woyesedwa wolungama uyutu, wosati uja ai; pakuti yense wakudzikuza yekha adzachepetsedwa; koma wodzichepetsa yekha adzakulitsidwa.
Yesu adalitsa ana
15 Ndipo anadza nao kwa Iye ana amakanda kuti awakhudze; koma pameneophunziraanaona anawadzudzula.
16 Koma Yesu anawaitana, nanena, Lolani ana adze kwa Ine, ndipo musawaletse; pakuti Ufumu wa Mulungu uli wa otere.
17 Indetu ndinena kwa inu, Aliyense wosalandira Ufumu wa Mulungu ngati mwana, sadzalowamo ndithu.
Mkulu mwini chuma
18 Ndipo mkulu wina anamfunsa Iye, nanena, Mphunzitsi wabwino, ndizichita chiyani, kuti ndilowe moyo wosatha?
19 Koma Yesu anati kwa iye, Unditcha Ine wabwino bwanji? Palibe wabwino, koma mmodzi, ndiye Mulungu.
20 Udziwa malamulo. Usachite chigololo, Usaphe, Usabe, Usachite umboni wonama, Lemekeza atate wako ndi amai ako.
21 Koma anati, Izi zonse ndazisunga kuyambira ubwana wanga.
22 Koma m’mene Yesu anamva, anati kwa iye, Usowa chinthu chimodzi: gulitsa zilizonse uli nazo, nugawire osauka; ndipo udzakhala nacho chuma chenicheni mu Mwamba; ndipo ukadze kuno, unditsate Ine.
23 Koma pakumva izi anagwidwa nacho chisoni chambiri; pakuti anali mwini chuma chambiri.
24 Ndipo Yesu pomuona iye anati, Ha! Nkuvutika nanga kwa anthu eni chuma kulowa Ufumu wa Mulungu!
25 Pakuti nkwapafupi kwangamiraipyole diso la singano koma kwa munthu mwini chuma, kulowa Ufumu wa Mulungu nkwapatali.
26 Koma akumvawo anati, Tsono ndani angathe kupulumutsidwa?
27 Koma Iye anati, Zinthu zosatheka ndi anthu zitheka ndi Mulungu.
28 Ndipo Petro anati, Taonani ife tasiya zathu za ife eni, ndipo takutsatani Inu.
29 Koma anati kwa iwo, Indetu ndinena kwa inu, Palibe munthu wasiya nyumba, kapena mkazi, kapena abale, kapena akum’bala, kapena ana, chifukwa cha Ufumu wa Mulungu,
30 koma adzalandira zobwezedwa koposatu m’nthawi ino; ndipo m’nthawi ilinkudza moyo wosatha.
Yesu aneneratu za mazunzo ake
31 Ndipo anadzitengera khumi ndi awiriwo, nati kwa iwo, Taonani, tikwera kunka kuYerusalemu, ndipo zidzakwaniritsidwa kwa Mwana wa Munthu zonse zolembedwa ndi aneneri.
32 Pakuti adzampereka kwaamitundu, nadzamseka, nadzamchitira chipongwe, nadzamthira malovu;
33 ndipo atamkwapula adzamupha Iye; ndipo tsiku lachitatu adzauka.
34 Ndipo sanadziwitse kanthu ka izi; ndi mau awa adawabisikira, ndipo sanazindikire zonenedwazo.
Msaona wa ku Yeriko
35 Ndipo kunali, pamene anayandikira ku Yeriko, msaona wina anakhala m’mbali mwa njira, napemphapempha;
36 ndipo pakumva khamu la anthu alinkupita, anafunsa, Ichi nchiyani?
37 Ndipo anamuuza iye, kuti, Yesu Mnazarayo alinkupita.
38 Ndipo anafuula, nanena, Yesu, Mwana wa Davide, mundichitire chifundo.
39 Ndipo iwo akutsogolera anamdzudzula iye, kuti akhale chete; koma iye anafuulitsa chifuulire, Mwana wa Davide, mundichitire chifundo.
40 Ndipo Yesu anaima, nalamulira kuti abwere naye kwa Iye; ndipo m’mene adafika pafupi, anamfunsa iye,
41 Ufuna ndikuchitire chiyani? Ndipo anati, Ambuye, kuti ndipenyenso.
42 Ndipo Yesu anati kwa iye, Penyanso: chikhulupiriro chako chakupulumutsa iwe.
43 Ndipo pomwepo anapenyanso, namtsata Iye, ndi kulemekeza Mulungu: ndipo anthu onse pakuona, anachitira Mulungu mayamiko.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/LUK/18-177d6c72454fe99c76e4209c6b65fd18.mp3?version_id=1068—