Za zolakwitsa, ndi makhululukidwe, ndi mphamvu ya chikhulupiriro ndi kutumikira kwathu
1 Ndipo anati kwaophunziraake, Sikutheka kuti zolakwitsa zisadze; koma tsoka iye amene adza nazo.
2 Kukolowekedwa mwala wamphero m’khosi mwake ndi kuponyedwa iye m’nyanja nkwapafupi, koma kulakwitsa mmodzi wa ang’ono awa nkwapatali.
3 Kadzichenjerani nokha; akachimwa mbale wako umdzudzule, akalapa, umkhululukire.
4 Ndipo akakuchimwira kasanu ndi kawiri pa tsiku lake, nakakutembenukira kasanu ndi kawiri ndi kunena, Ndalapa ine; uzimkhululukira.
5 Ndipoatumwianati kwa Ambuye, Mutionjezere chikhulupiriro.
6 Koma Ambuye anati, Mukakhala nacho chikhulupiriro ngati kambeu kampiru, mukanena kwa mtengo uwu wamkuyu, Uzulidwe, nuokedwe m’nyanja; ndipo ukadamvera inu.
7 Koma ndani mwa inu ali naye kapolo wolima, kapena woweta nkhosa, amene pobwera iye kuchokera kumunda adzanena kwa iye, Lowa tsopano, khala pansi kudya;
8 wosanena naye makamaka, Undikonzere chakudya ine, nudzimangire, nunditumikire kufikira ndadya ndi kumwa; ndipo nditatha ine udzadya nudzamwa iwe?
9 Kodi ayamika kapoloyo chifukwa anachita zolamulidwa?
10 Chotero inunso m’mene mutachita zonse anakulamulirani, nenani, Ife ndife akapolo opanda pake, tangochita zimene tayenera kuzichita.
Yesu achiritsa akhate khumi
11 Ndipo kunali, pakumuka kuYerusalemuIye analikupita pakati pa Samariya ndi Galileya.
12 Ndipo m’mene analowa Iye m’mudzi wina, anakomana naye amuna khumi akhate, amene anaima kutali;
13 ndipo iwo anakweza mau, nanena, Yesu, Mbuye, mutichitire chifundo.
14 Ndipo pakuwaona anati kwa iwo, Pitani, kadzionetseni nokha kwa ansembe. Ndipo kunali, m’kumuka kwao, anakonzedwa.
15 Ndipo mmodzi wa iwo, pakuona kuti anachiritsidwa, anabwerera m’mbuyo, nalemekeza Mulungu ndi mau aakulu;
16 ndipo anagwa nkhope yake pansi kumapazi ake, namyamika Iye; ndipo analiMsamariyaameneyo.
17 Ndipo Yesu anayankha nati, Kodi sanakonzedwe khumi? Koma ali kuti asanu ndi anai aja?
18 Akubwera kulemekeza Mulungu sanapezeke mmodzi kodi, koma mlendo uyu?
19 Ndipo anati kwa iye, Nyamuka, nupite; chikhulupiriro chako chakupulumutsa iwe.
Za kufikanso kwa Ambuye
20 Ndipo pameneAfarisianamfunsa Iye, kuti, Ufumu wa Mulungu ukudza liti, anawayankha, nati, Ufumu wa Mulungu sukudza ndi maonekedwe;
21 ndipo sadzanena, Taonani uwu, kapena uwo! Pakuti, taonani, Ufumu wa Mulungu uli m’kati mwa inu.
22 Ndipo anati kwa ophunzira ake, Adzadza masiku, amene mudzakhumba kuona limodzi la masiku aMwana wa Munthu, koma simudzaliona.
23 Ndipo adzanena ndi inu, Taonani ilo! Taonani ili? Musachoka kapena kuwatsata;
24 pakuti monga mphezi ing’anipa kuchokera kwina pansi pa thambo, niunikira kufikira kwina pansi pa thambo, kotero adzakhala Mwana wa Munthu m’tsiku lake.
25 Koma ayenera ayambe wamva zowawa zambiri nakanidwe ndi mbadwo uno.
26 Ndipo monga kunakhala masiku a Nowa, momwemo kudzakhalanso masiku a Mwana wa Munthu.
27 Anadya, anamwa, anakwatira, anakwatiwa, kufikira tsiku lija Nowa analowa m’chingalawa, ndipo chinadza chigumula, nkuwaononga onsewo.
28 Monga momwenso kunakhala masiku a Loti; anadya, anamwa, anagula, anagulitsa, anabzala, anamanga nyumba;
29 koma tsiku limene Loti anatuluka mu Sodomu udavumba moto ndisulufurezochokera kumwamba, ndipo zinawaononga onsewo;
30 momwemo kudzakhala tsiku lakuvumbuluka Mwana wa Munthu.
31 Tsikulo iye amene adzakhala pamwamba pa tsindwi, ndi akatundu ake m’nyumba, asatsike kuwatenga; ndipo iye amene ali m’munda modzimodzi asabwere ku zake za m’mbuyo.
32 Kumbukirani mkazi wa Loti.
33 Iye aliyense akafuna kusunga moyo wake adzautaya, koma iye aliyense akautaya, adzausunga.
34 Ndinena ndi inu, usiku womwewo adzakhala awiri pa kama mmodzi; mmodzi adzatengedwa, ndi wina adzasiyidwa.
35 Padzakhala akazi awiri akupera pamodzi, mmodzi adzatengedwa, ndi wina adzasiyidwa.
37 Ndipo anayankha nanena kwa Iye, Kuti, Ambuye? Ndipo anati kwa iwo, Pamene pali mtembo, pomweponso miimba idzasonkhanidwa.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/LUK/17-8aaea162cdb9799223cee29e0895bfe8.mp3?version_id=1068—